< Ecclesiastes 1 >
1 Pa inge kas lun sie Mwet Luti Lalmwetmet, wen natul David, su tuh tokosra in Jerusalem.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Mwet Luti Lalmwetmet el fahk lah ma nukewa ma lusrongten na lusrongten! Moul uh wangin sripama na lusrongten se.
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Kom orekma ac kemkatu in moul lom nufon, na mea oasr ma kom konauk kac?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 Sie fwil uh somla ac sie fwil sifil tuku, a faclu nuna ouiya ah na.
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 Faht ah srakna tak ac srakna tili, na sa na in folok nu ke acn se ma el ac sifil takak we.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Eng uh tuh eir me ac som nu epang, ac sifil tuk — raun na raun.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Infacl nukewa sororla nu meoa, a meoa soenna sessesla. Kof uh folok nu yen infacl uh mutawauk we, ac sifilpa sororma.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 Saflaiyen ma nukewa pa totola — sie totola na yohk su wangin kas fal in aketeya. Mutasr tia muti ke ma kut liye, ac insresr tia muti ke ma kut lohng.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 Ma sikyak meet ac sifilpa sikyak. Ma orekla tari ac sifilpa orek. Wangin ma sasu in faclu nufon.
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 Mwet uh fahk, “Liye, ma sasu se pa inge!” Tusruktu sutuu, sikyak tari meet, oemeet liki na kut isusla ah.
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Wangin mwet esam ma tuh sikyak in pacl meet ah, ac in pacl fahsru wangin mwet fah esam ma sikyak in len ingela.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Nga, Mwet Luti Lalmwetmet, su tuh muta Jerusalem ac tokosra fin acn Israel nufon.
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 Nga nunkala ku sik mu nga ac tuni ac lutlut ke ma nukewa ma mwet uh oru fin faclu. God El ase orekma na toasr nu sesr mwet uh in oru.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Nga liye tari ma nukewa ma orek faclu, ac nga fahk nu sum, nufonna wangin sripaoana ukweyen eng uh.
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 Kom tia ku in aksuwosyela ma kihla; kom tia pac ku in oek ma wangin uh.
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Nga fahk nu sik sifacna, “Nga sie mwet na fulat, ac nga arulana lalmwetmet liki kutena mwet su leumi Jerusalem meet likiyu. Nga etu na pwaye lah mea lalmwetmet ac etauk.”
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 Nga tuh sulela ku sik in etu ke kalmen etauk ac kalmen lalfon, oayapa ke lalmwetmet ac wel. Tusruktu nga konauk lah ma inge oana ukweyen eng uh.
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 Lalmwetmet lom fin yokelik, na fosrnga lom ac yokelik pac. Fin yokelik etauk lom, ac yokelik pulakinyen keok sum.
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.