< Deuteronomy 30 >

1 “Inge nga sot nu suwos tuh kowos in sulela inmasrlon mwe insewowo ac mwe selnga. Ke pacl se ma inge nukewa ac sikyak nu suwos, ac kowos muta inmasrlon mutunfacl yen LEUM GOD lowos El akfahsryekowoselik nu we, kowos ac esamak sulela se inge ma nga sot nu suwos.
Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
2 Kowos, ac fwilin tulik nutuwos, fin foloko nu yurin LEUM GOD ac akos ma sap lal su nga sot nu suwos misenge ke insiowos nufon,
ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
3 na LEUM GOD lowos fah pakomutowos. El ac fah folokinkowosme liki mutunfacl nukewa El akfahsryekowoselik nu we, ac El ac sifilpa folokonak moul in insewowo lowos meet ah.
pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
4 Kowos finne fahsrelik nu yen loessula faclu, LEUM GOD lowos El ac fah eiskowoseni nu sie ac folokinkowosme
Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
5 kowos in mau ku in sifilpa eis suwos facl se ma mwet matu lowos tuh muta we meet ah. Oayapa El ac fah oru tuh kowos in kasrup liki, ac pus liki, fwil lun papa matu tomowos meet ah.
Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
6 LEUM GOD lowos El ac sot nu suwos ac fwilin tulik nutuwos inse akosten, tuh kowos in lungse El ke insiowos nufon, ac kowos fah mutana in facl sac.
Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
7 El ac fah furokla mwe selnga inge nukewa tuh in ma nu sin mwet lokoalok lowos, su tuh srungakowos ac akkeokye kowos.
Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
8 Na kowos fah sifilpa aksol ac liyaung ma sap lal nukewa ma nga sot nu suwos misenge.
Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
9 LEUM GOD El ac fah akinsewowoye kowos in ma nukewa kowos oru — ac fah puseni tulik nutuwos ac cow nutuwos, ac ima lowos ac fah isus fahko puspis. El ac fah arulana engan in oru tuh kowos in kapkapak oana ke El tuh oru nu sin papa matu tomowos.
Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
10 Tusruktu kowos ac enenu in aksol ac liyaung ma sap nukewa ma simla in book in ma sap lal inge. Kowos fah enenu in forla nu sel ke insiowos nufon.
ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
11 “Ma nga sapkin nu suwos misenge tia upala nu suwos, ku ma kowos ac koflana in oru.
Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
12 Tia oasr oe inkusrao. Kowos tia enenu in siyuk, ‘Su fah utyak ac usya ma sap inge nu yorosr, kut in ku in lohng kac ac akos?’
Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
13 Tia pac oan lac meoa ingo. Kowos tia enenu in siyuk, ‘Su fah som fin kof uh lac ac use nu yorosr, kut in ku in lohng kac ac akos?’
Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
14 Mo, oasr na yuruwos inge. Kowos etu kac, ac ku na in fahk ke oaluwos. Ouinge kowos in akos.
Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
15 “Misenge nga sot tuh kowos in sulela inmasrlon ma wo ac ma koluk; inmasrlon moul ac misa.
Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
16 Nga sapkin nu suwos misenge tuh kowos in lungse LEUM GOD lowos, ac aksol, ac liyaung ma sap lal, oakwuk lal, ac nununku lal nukewa, na kowos ac fah kapkapak ac orala sie mutunfacl lulap. LEUM GOD lowos fah akinsewowoye kowos in facl se su kowos apkuran in oakwuki we.
Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
17 “Tusruktu kowos fin seakos ac srangesr lohng kas, ac fahsr tokolos su alu nu ke god saya,
Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
18 nga fahkak kalem nu suwos lah kowos ac fah kunausyukla. Kowos ac tia moul paht fin facl se ingo ma kowos apkuran in alukela Infacl Jordan in utyak ac oakwuki we.
lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
19 Inge nga sot tuh kowos in sulela inmasrlon moul ac misa, inmasrlon insewowo lun God ac selnga lun God, ac nga pang nu sin kusrao ac faclu in orek loh ke sulela lowos. Kowos in sulela moul.
Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
20 Lungse LEUM GOD lowos, ac aksol, ac kowos in inse pwaye nu sel, na kowos, ac fwilin tulik nutuwos, fah moul paht fin facl se su El tuh wulela kac mu El ac sang nu sin papa matu tomowos — Abraham, Isaac, ac Jacob.”
Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.

< Deuteronomy 30 >