< Deuteronomy 15 >

1 “Ke yac akitkosr nukewa, kowos fah sisla soemoul lalos nukewa su soemoul nu suwos ke mani.
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 Kowos ac oru ouinge: Kutena mwet su sang mani nu sin sie mwet Israel wial, elan sisla soemoul sac; el fah tia srike in eisla sel, mweyen LEUM GOD El fahk tari in sisila soemoul uh.
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 Kowos ku in sap mwetsac nukewa in folokonot soemoul lalos nu suwos, tusruktu kowos tia enenu in eis soemoul lun mwet Israel wiowos.
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 “LEUM GOD lowos El ac fah akinsewowoye kowos in facl se su El sot nu suwos. Wangin sie suwos ac fah sukasrup,
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 kowos fin aksol ac arulana karinganang in oru ma nukewa nga sapkin nu suwos misenge.
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 LEUM GOD El fah akinsewowoye kowos, oana ke El wulela. Kowos fah sang mani nu sin mutunfacl puspis su elos ac fah enenu in folokonot, tusruktu kowos fah tia enenu in ngusr mani selos. Kowos fah leumi mutunfacl puspis, tusruktu wangin mutunfacl ac fah leum fowos.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 “Fin oasr sie mwet Israel muta in enenu in kutena siti ke facl se ma LEUM GOD lowos El asot nu suwos, kowos in tia nunku keiwos sifacna, a kowos in kasrel.
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 Kowos in kulang ac engan in sang kutena enenu lal, na el ac fah folokonot tok.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 Kowos in tia srangesr sang mwe enenu lal an mweyen yac se akitkosr — yac in sisila soemoul uh — apkuranme. Nimet lela nunak koluk ouinge in oan in kowos. Kowos fin srunga sang enenu lun sie mwet Israel wiowos, el ac pang nu sin LEUM GOD lain kowos, ac kowos ac eis mwata.
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 Sang enenu lal an ke inse engan, tia ke inse toasr, na LEUM GOD El fah akinsewowoye kowos ke ma nukewa kowos oru.
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 Pacl nukewa ac oasr kutu mwet Israel su sukasrup ac muta in enenu, pa sis nga sapkin kowos in kulang nu selos ac kasrelos.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 “Sie mwet Israel wiom, mukul ku mutan, fin sifacna kukakunul nu sum tuh elan mwet kohs lom, kom tufah fuhlella tukun el kulansupwekom ke yac onkosr. Ke sun yac se akitkosr, kom enenu in aksukosokyalla.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 Na ke kom fuhlella elan sukosokla, nimet supwalla pisinpo.
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 Sang nu sel sheep ac nani, wheat ac wain, fal nu ke lupan ma LEUM GOD El akinsewowoye kom kac.
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 Esam lah kowos tuh mwet kohs in Egypt, ac LEUM GOD lowos El molikowosla, pa oru nga sot ma sap se inge nu suwos.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 “Tusruktu mwet kohs lom an fin lungse kom ac sou lom, sahp el ac tia lungse som liki kom, a el ac kena mutana yurum.
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 Fin ouinge, usalla nu ke srungul in lohm sum, ac putala sie pat ah ke sracl, na el ac fah mwet kohs lom ke lusenna moul lal. Oru oapana nu sin mutan kohs lom.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 Nik kom inse toasr ke kom aksukosokyela sie mwet kohs lom, mweyen ke yac onkosr el tuh orekma nu sum ke tafunna molin sie mwet kulansap. Oru ouinge, na LEUM GOD El fah akinsewowoye kom in ma nukewa kom oru.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 “Srela nu sin LEUM GOD lowos wounse mukul ke cow ac sheep nutuwos. Nimet sang cow inge in orekma, ac nimet kal unen sheep inge.
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 Ke kais sie yac, kowos ac sou lowos in kang ma inge ye mutun LEUM GOD ke acn sefanna ma El sulela kowos in alu nu sel we.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 Tusruktu kosro inge fin ul, ku kun, ku oasr kutena ma koluk yohk ke manolos, kowos fah tia kisakin nu sin LEUM GOD lowos.
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 Kowos ku in kang kosro ouinge in lohm suwos. Finne mwet ma aknasnasyeyukla ku tia, kowos nukewa ku in kang, oana ke kowos kang deer ku antelope.
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Tusruktu nimet kang srah kac — kowos in okoala nu infohk uh oana kof uh.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

< Deuteronomy 15 >