< Luo Samuel 3 >

1 Arulana paht mweun se inmasrlon mwet mweun kasreyen sou lal Saul ac mwet mweun kasreyal David. In pacl se inge ku lal David yokyokelik, a ku lun mwet lainul sriksrikeni.
Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
2 Wen onkosr natul David inge takla ke matwalos, elos isusla in acn Hebron: Amnon — nina kial pa Ahinoam, mutan Jezreel;
Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
3 Chileab — nina kial pa Abigail, mutan Carmel katinmas kial Nabal; Absalom — nina kial pa Maacah, acn natul Talmai, tokosra lun Geshur;
Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
4 Adonijah — nina kial pa Haggith; Shephatiah — nina kial pa Abital;
wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
5 Ithream — nina kial pa Eglah. Wen natul inge kewa isusla in acn Hebron.
ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
6 Ke mweun uh srakna orek inmasrlon mwet mweun lal David ac mwet mweun kasreyen sou lal Saul, Abner el kui na kui inmasrlon mwet mweun lal Saul.
Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
7 Sie len ah, Ishbosheth wen natul Saul, el akkolukyal Abner fahk mu el motul yorol Rizpah, mutan kulansap kial Saul, su acn natul Aiah.
Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
8 Ma se inge oru Abner el kasrkusrak ac fahk, “Ku kom nunku mu nga ku in oru koluk nu sel Saul? Mea pwaye lah kom pangon mu nga kulansupu mwet Judah? Oemeet me nga nuna pwayena nu sel Saul, papa tomom, oayapa mwet wial ac kawuk lal, ac nga pa pwanang kom tia kutangyukla sel David. A misenge kom akkolukyeyu ke sripen mutan se?
Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
9 Lela God Elan sringilyuwi ngan misa, nga fin tia akpwayeye ma nga fahk inge: nga fah oru oana wulela lun LEUM GOD nu sel David,
Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
10 in eisla tokosrai lukel Saul ac fita lal, ac sang nu sel David tuh elan tokosra fin acn Israel ac Judah, mutawauk e Dan nu epang fahla nwe Beersheba nu eir!”
Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
11 Ishbosheth el arulana sangeng sel Abner, oru el tia ku in fahkla sie kas.
Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
12 Abner el supwala mwet utuk kas nu yorol David, su muta Hebron in pacl sac, tuh elos in siyuk, “Su ac leumi facl se inge uh? Kom fin orala sie wulela nu sik, na nga ac fah kasrekom eisla acn Israel nufon lom.”
Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
13 David el fahk, “Wona. Nga ac orala sie wulela nu sum kom fin orala ma se inge: usalu Michal, acn natul Saul, ke kom ac tuku.”
Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
14 Ac David el oayapa supwala mwet utuk kas nu yorol Ishbosheth ac fahk, “Folokunulma Michal, mutan kiuk. Nga molella tari ke siofok kulun ma mukul lun mwet Philistia, tuh elan mutan kiuk.”
Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
15 Na Ishbosheth el sap utuku mutan sac lukel Paltiel, mukul tumal, wen natul Laish.
Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
16 Paltiel el fahsr na tung tokol nwe ke siti srisrik Bahurim. Tusruktu ke Abner el sap elan folokla, na Paltiel el folokla.
Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
17 Abner el som nu yurin mwet kol lun Israel ac fahk nu selos, “Kowos tuh kena David elan tokosra lowos ke pacl na loes.
Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
18 Inge pacl wo lowos. Esam lah LEUM GOD El tuh fahk, ‘Nga ac orekmakunul David, mwet kulansap luk, tuh elan molela mwet luk Israel liki mwet Philistia ac liki mwet lokoalok lalos saya nukewa.’”
Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
19 Abner el kaskas pac nu sin mwet in sruf lal Benjamin, na el som nu Hebron in fahkang nu sel David ma mwet in sruf lal Benjamin ac mwet Israel insesela in oru.
Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
20 Ke Abner el tuku nu yorol David in acn Hebron wi mwet longoul, David el orala kufwa se nu selos.
Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
21 Abner el fahk nu sel David, “Leuwa, inge nga ac som ac eisani mwet Israel nukewa in mwet lom. Elos ac fah eis kom in tokosra lalos, na kom ac fah leum fin mutunfacl sac nufon, fal nu ke lungse lom.” David el wulela na ku nu sel Abner lah el ac muta in misla, na el supwalla inkanek lal.
Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
22 Tok, Joab ac mwet pwapa saya lal David elos folokla liki mweun, ac elos us ma wap pukanten welulos. Tusruktu Abner el tila muta Hebron yorol David, mweyen David el supwalla wi sie wulela ke misla.
Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
23 Ke Joab ac mwet lal ah sun acn we, fwackyang nu sel lah Abner el tuku nu yorol Tokosra David, ac supweyukla el tari, wi wulela ke misla.
Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
24 Ouinge Joab el som nu yurin tokosra ac siyuk sel, “Mea se kom orala uh? Abner el tuku nu yurum, ac efu ku kom fuhlella elan som?
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
25 Nga lulalfongi lah kom etu na lah el tuku in na kiapwekom, ac in etu ke ma nukewa kom oru uh ac yen nukewa kom fahsr nu we!”
Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
26 Tukun Joab el som lukel David, el supwala mwet in tuh usalu Abner, ac elos folokunulma liki luf in Kof Sirah. Tusruktu David el tia etu kac.
Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
27 Ke Abner el sun acn Hebron, Joab el kololla nu sisken mutunpot lun siti sac oana elan ke sramsram lukma nu sel. Na Joab el fakisya insial Abner. Ouinge akmuseyuki Abner mweyen el tuh unilya Asahel, tamulel lal Joab.
Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
28 Ke David el lohngak pweng sac, el fahk, “LEUM GOD El etu lah wangin mwetik ac mwet luk ke misa lal Abner.
Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
29 Lela tuh folokinyen ma koluk se inge in oan facl Joab ac sou lal nufon. Lela in oasr mukul se in fwil nukewa in sou lal weak mas koluk, ku musen leper, ku elahn mutan, ku misa ke mweun, ku sufal mongo nal.”
Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
30 Ouinge Joab ac Abishai tamulel lal, eltal foloksak ac unilya Abner ke sripen el tuh unilya Asahel tamulel se laltal, ke mweun in acn Gibeon.
(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
31 Na David el sap Joab ac mwet lal ah in salik nuknuk lalos, ac nokomang nuknuk yohk eoa in akkalemye asor lalos kacl Abner. Ke pacl in pukmas, Tokosra David sifacna el fahsr tukun box in mas sac.
Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
32 Abner el pukpuki Hebron, ac tokosra el tung ke pusra lulap ke kulyuk ah, ac mwet nukewa wi pac tung.
Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
33 David el onkin on in eoksra soko inge kacl Abner: “Efu ku Abner elan misa oana mwet lalfon se?
Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34 Paol tia kapiri, Ac nial tiana losyukeni. El misa oana misa lun sie mwet anwuki sin mwet koluk!” Na mwet uh sifilpa tung kacl.
Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
35 In len sac nufon, mwet uh srike in oru David elan kangla kutu mongo, tuh el na orala sie wulela na ku mu, “Lela Leum God Elan sringilyuwi ngan misa nga fin kangla kutena ma meet liki fongeni!”
Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
36 Ke mwet uh elos liye ma inge elos insewowo kac. Aok, ma nukewa tokosra el oru, mwet uh insewowo kac.
Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
37 Mwet lal David nukewa ac mwet Israel nukewa kalem kac lah wangin ip lal Tokosra David ke misa lal Abner.
Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
38 Ac tokosra el fahk nu sin mwet pwapa lal, “Mea, kowos tia akilen lah sie mwet kol fulat lun Israel el misa misenge?
Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
39 Nga finne tokosra su sulosolla sin Leum God, tuh nga pulakin munas misenge. Wen ekasr natul Zeruiah inge upala lokoalok lalos in nunak luk. Lela LEUM GOD Elan kalyaelos fal nu ke orekma koluk elos oru inge!”
Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

< Luo Samuel 3 >