< Luo Samuel 20 >

1 In pacl se inge oasr sie mwet lusrongten in acn Gilgal — inel pa Sheba wen natul Bikri, ac el ma in sruf lal Benjamin. El ukya mwe ukuk ac wowoyak ac fahk, “Sisella David! Kut ac tia welul! Mwet Israel nukewa, kut som nu yen sesr ah!”
Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
2 Ouinge mwet Israel elos sisella David, ac welulla Sheba. A mwet Judah elos insese na yorol David, ac elos welul fahla Infacl Jordan lac nu Jerusalem.
Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
3 Ke David el tuku nu lohm sin tokosra in acn Jerusalem, el orani mutan kulansap singoul kial ma el tuh filiya in liyaung inkul sel ah, ac eisalosyang nu inpoun mwet topang uh. El sang enenu lalos, tuh el tia oan yorolos. Elos muta kaul ac moul oana mutan katinmas ke lusen moul lalos.
Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
4 Ac tokosra el fahk nu sel Amasa, “Pangoneni mwet Judah ac welulos foloko nu inse inge ulela.”
Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
5 Amasa el som in pangnolos, tuh el tia foloko ke pacl se tokosra el tuh fahk nu sel ah.
Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
6 Na tokosra el fahk nu sel Abishai, “Sheba el ac orek lokoalok nu sesr yohk lukel Absalom. Us mwet luk an ac fahsrot ukwal, elan ma tia utyak nu in siti oasr pot ku we pwanang kut ac kofla sruokilya.”
Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
7 Ke ma inge, mwet lal Joab ac mwet topang oayapa mwet mweun nukewa saya, elos welul Abishai som liki acn Jerusalem in ukwal Sheba.
Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
8 Ke elos sun eot lulap se in acn Gibeon, Amasa el sonolos. Joab el nukum nuknuk in mweun, ac cutlass se oan ke ma neinya sripsrip ke pel lal. Ke el fahsr nu meet, cutlass sac putatla.
Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
9 Joab el fahk nu sel Amasa, “Ma lik, kom fuka?” ac el sruokya alut lal ah ke lac po layot tuh elan ngok mutal.
Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
10 Amasa el tiana akola nu ke cutlass se ma Joab el sruokya ke lac paol lasa, na Joab el fakisya insial ac koanonsial raki nu infohk uh. Na el misa na insac, pwanang Joab el tia enenu in faksilya pacl luo. Na Joab ac Abishai tamulel lal, som in ukwal Sheba.
Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
11 Sie sin mwet lal Joab ah tui ke manol Amasa ac wola fahk, “Mwet nukewa su ma lal Joab ac David, fahsr tokol Joab!”
Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
12 Manol Amasa afla ke srah ac oanna inkanek ah. Sie mwet lal Joab liye lah mwet uh fahsr tui ke mano sac, na el amakunla liki innek ah nu inimae, ac afinya ke kaot se.
Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
13 Tukun mano sac mokleyukla liki innek ah, na mwet nukewa fahsr tokol Joab in ukwal Sheba.
Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
14 Sheba el fahsr alukela acn sin sruf nukewa lun Israel, ac tuku nu ke siti Abel Beth Maacah, ac mwet nukewa in sou lal Bikri elos toeni ac fahsr tokol nu in siti uh.
Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
15 Mwet lal Joab elos lohng lah Sheba el oasr we, na elos fahsreni kuhlusya siti sac. Elos sang fohk musaeak nien fanyak lalos nu fin pot we, ac mutawauk in pikin ye pot uh in raki.
Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
16 Oasr mutan lalmwetmet se in siti sac, su wowoyak fin pot ah, ac fahk, “Koasrlong! Lohng! Sap Joab elan fahsru. Nga ke sramsram nu sel.”
mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
17 Na Joab el som nu yorol, ac mutan sac siyuk, “Ku kom pa Joab?” Na Joab el fahk, “Aok, nga.” Na mutan sac fahk, “Lohng ma nga ac fahk uh.” Na Joab el fahk, “Nga ac lohng.”
Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
18 Mutan sac fahk, “Oasr kas se lun mwet in pacl somla fahk mu, ‘Fahla eis top lom an in siti lun Abel’ — na pa ingan ma elos tuh oru.
Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
19 Siti se sesr inge siti na pwengpeng se. Yohk misla ac insese lasr nu sin tokosra lasr inmasrlon siti Israel nukewa. Efu kom ku srike in kunausla? Ku kom lungse akkolukyela ma lun LEUM GOD?”
Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
20 Na Joab el topuk, “Mo! Tiana ku! Nga tia ku in akkolukye ku kunausla siti lowos uh!
Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
21 Tia pa ingan ma kut akoo. Oasr sie mukul, inel pa Sheba wen natul Bikri, el tuku liki eol uh in facl Ephraim, ac el mutawauk sie alein lainul Tokosra David. Usalu mwet se ingan, na nga fah som liki siti lowos uh.” Na mutan sac fahk, “Kut ac sisot sifal fin pot uh wot nu sum.”
Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
22 Na el som nu yurin mwet in siti sac ac fahkak nunak lal nu selos, na elos pakela sifal Sheba ac sisla fin pot uh lac nu sel Joab. Joab el ukya mwe ukuk in akkalemye nu sin mwet lal elos in som liki siti uh, na elos folokla nu yen selos. Ac Joab el folokla nu Jerusalem nu yorol tokosra.
Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
23 Joab el captain lun un mwet mweun lun Israel. Benaiah wen natul Jehoiada, pa liyaung un mwet topang lal David.
Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
24 Adoniram pa liyaung orekma lun mwet kohs. Jehoshaphat wen natul Ahilud, pa karinganang ma simla.
Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
25 Sheva pa mwet sim inkul lun tokosra. Zadok ac Abiathar pa mwet tol.
Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
26 Ac Ira, sie mwet liki siti Jair, el oayapa sie sin mwet tol lal David.
ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.

< Luo Samuel 20 >