< Luo Samuel 18 >

1 Tokosra David el eisani mwet lal nukewa ac kitalik nu ke u — ke kais tausin, ac kais foko, ac sang mwet kol in sapsap nu selos.
Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
2 Na el supwalosla ke u tolu. Captain lun kais sie u inge pa Joab, ac Abishai tamulel lal Joab, ac Ittai mwet Gath. Ac tokosra el fahk nu sin mwet lal inge, “Nga sifacna ac wi kowos pac.”
Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
3 Na elos fahk nu sel, “Tia fal kom in wi kut som. Kut nukewa fin forla kaingla, ac wangin kalmac nu sin mwet lokoalok lasr. Ku tafu sesr fin misa, ac fah ma pilesr pac selos. Kom mukefanna saok liki singoul tausin sesr, na pa wo kom in mutana in siti uh ac supu mwe kasru nu sesr.”
Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
4 Tokosra el topuk, “Ma na kowos wotela an, nga ac wi na.” Na el tuyak ke mutunpot in siti sac ke mwet lal ah illa ke u lalos, kais tausin ac kais foko ke u se.
Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
5 El sapkin nu sel Joab, Abishai ac Ittai, ac fahk, “Ke sripuk, nimet oru kutena ma koluk nu sin mwet fusr sac, Absalom.” Mwet mweun nukewa elos lohng ke David el sapkin nu sin captain tolu lal.
Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
6 Mwet mweun lal David elos illa nu inimae, ac mweuni mwet Israel ke insak Ephraim.
Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
7 Mwet Israel elos kutangyukla sin mwet lal David. Arulana upa mweun sac. Oasr mwet longoul tausin misa in len sac.
Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
8 Mweun sac fahsrelik in polo acn sac nufon, ac pisen mwet misa insak ah pus liki mwet anwuki ke mweun ah.
Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
9 Na Absalom el sun kutu mwet lal David. Absalom el muta fin miul soko, ac ke el kasrusr ye sak oak lulap soko, insifal sremla ke lesak ah. Miul soko ah kasrusr na, a Absalom el atlana ke sak oak soko ah.
Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
10 Sie sin mwet lal David ah liyalak ac fahkang nu sel Joab, “Nga liyalak Absalom el oan atla ke sak oak soko!”
Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
11 Ac Joab el fahk, “Fin pwaye kom liyal, efu kom ku tia unilya na we? Nga lukun sifacna sot singoul ipin silver ac sie pel lom.”
Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
12 Mwet sac fahk, “Kom finne ase sie tausin ipin silver, a nga tia ku in srukak soko kufinpouk in lain wen natul tokosra. Kut nukewa lohng ke tokosra el sapkin nu sum Abishai ac Ittai, ac fahk, ‘Ke sripuk, nimet oru kutena ma koluk nu sin mwet fusr sac, Absalom.’
Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
13 Tusruktu nga funu seakos tokosra ac unilya Absalom, tokosra el lukun lohngak kac mweyen el lohng ma nukewa, na kom lukun tiana kasreyu.”
Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
14 Joab el fahk, “Nga ac tia sifil sisla pacl luk yurum.” Na el us osra tolkwe ac sang fakisya iniwal Absalom ke el srakna moul oan atla ke sak oak soko ah.
Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
15 Ac singoul sin mwet mweun lal Joab elos apnulla Absalom ac faksilya nwe ke el misa.
Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
16 Joab el sap elos in ukya mwe ukuk in tui mweun ah, na mwet lal ah foloko ac tila ukwe mwet Israel.
Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
17 Elos us manol Absalom, ac sisya in sie luf na loal insak ah, ac sisang yol in eot na lulap in afinya. Mwet Israel nukewa elos kaingla, kais sie mwet nu yen sel.
Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
18 Ke Absalom el tuh srakna moul, el tulokunak soko sru lulap ke Infahlfal Tokosra, in tuh sie mwe esmak kacl sifacna, mweyen wangin tulik natul in us inel tuh in tia wanginla. Ouinge el sang inel sifacna nu ke sru soko ah, na srakna eteyuk sru soko ah nwe misenge mu Mwe Esmakin Lal Absalom.
Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
19 Na Ahimaaz, wen natul Zadok, el fahk nu sel Joab, “Lela ngan kasrusr nu yorol tokosra ac us pweng wo se inge lah LEUM GOD El molella liki mwet lokoalok lal ah.”
Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
20 Na Joab el fahk, “Mo! Kom fah tia us kutena pweng misenge. Kom ku in us ke sie na len, tuh tia misenge, mweyen wen nutin tokosra el misa.”
Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
21 Na el fahk nu sin mwet kohs se lal su sie mwet Ethiopia, “Fahla fahk nu sin tokosra ma kom liye ah.” Na mwet kohs sac srimi ac kasrusr som.
Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
22 Na Ahimaaz el sifil kwafe ac fahk, “Nga mansis ma nukewa, tuh nga siyuk nunak munas, lela ngan wi pac usyen pweng sacn.” Joab el siyuk, “Wen nutik, efu ku kom lungse us pweng sacn, ke ac wangin molo nu sum?”
Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
23 Na Ahimaaz el sifilpa fahk, “Finne mea ma ac sikyak, nga srakna lungse wi kom.” Joab el fahk, “Kwal, fahla.” Ouinge Ahimaaz el kasrusr tufoki inkanek soko ke Infahlfal Jordan, ac el alukella mwet kohs sac.
Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
24 Oasr pot luo raunela siti sac, ac David el muta inmasrlon mutunpot se lik ac mutunpot se loac. Sie mwet topang el fanyak nu fin pot uh, ac tu fin mutunpot sac. Ke el ngetla el liyauk mwet se mukena yume.
Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
25 El pang ac fahk nu sin tokosra, ac tokosra el fahk, “El fin mukena, el us pweng wo.” Mwet kasrusr sac el yume na.
Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
26 Na mwet topang sac liyauk sie pac mwet su mukena kasrusr, na el ngeti ac pang nu sin mwet se liyaung mutunoa, “Ngetla liye! Mwet se pa pac yume uh!” Na tokosra el fahk, “El us pac pweng wo.”
Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
27 Mwet topang sac fahk, “Nga liye tuh mwet se meet ah kasrusr oana Ahimaaz.” Tokosra el fahk, “El mwet na wo se, ac el us pweng wo.”
Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
28 Ahimaaz el wola ac paing nu sin tokosra, ac el putati nu infohk ah ye mutal ac fahk, “Leum luk, kaksakin LEUM GOD lom su asot kutangla nu sum fin mwet lokoalok lom!”
Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
29 Tokosra el siyuk, “Ya Absalom nutik ah ku na?” Ahimaaz el topuk, “Ke Joab, captain lom, el supweyume, nga tuh liye oasr mukuikui yohk se orek tuh nga tia ku in etu lah mea se.”
Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
30 Tokosra el fahk nu sel, “Fahsrot tu inse ingo.” Ac el fahla nu insac ac tu we.
Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
31 Na mwet Ethiopia sac el tuku, ac fahk nu sin tokosra, “Leum fulat, oasr pweng wo se nga us nu sum! Misenge LEUM GOD El asot kutangla nu sum fin mwet nukewa su tuyak lain kom!”
Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
32 Ac tokosra el siyuk, “Ya Absalom nutik ah ku na?” Mwet kohs sac fahk, “O Tokosra, leum luk, nga kena tuh ma sikyak nu sel ah in sikyak nu sin mwet lokoalok lom nukewa, oayapa nu sin mwet nukewa su lain kom.”
Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
33 Ac insien tokosra sessesla ke asor. El fanyak nu ke infukil se oan lucng ke mutunpot ah, ac tung. Ke el tung el fahk, “We, wen nutik! Wen nutik, Absalom! Absalom nutik! Nga ke in nga pa misa ac tia kom, wen nutik! Absalom nutik!”
Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”

< Luo Samuel 18 >