< Luo Samuel 16 >

1 Ke David el fahsr sasla mangon tohktok uh, el sa na sonol Ziba, mwet kulansap lal Mephibosheth. Ziba el us donkey lukwa nwanala fintokoltal ke bread luofoko, tun in raisin siofok, ung in fokinsak siofok, ac sie pak orekla ke kulun kosro sessesla ke wain.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 Tokosra David el siyuk sel, “Mea kom ac oru ke ma ingan uh?” Ziba el fahk, “Leum luk, donkey inge ma kom ac sou lom an in kasrusr fac, na bread ac fokinsak inge ma mwet uh in kang, ac wain uh ma elos in nim ke elos ac totola yen mwesis.”
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 Na tokosra el siyuk sel, “El aya Mephibosheth, wen se nutin natul Saul, leum lom?” Ac Ziba el fahk, “El muta oasr Jerusalem, mweyen oasr lulalfongi lal mu inge mwet Israel elos ac folokonang nu sel tokosrai lal Saul, papa matu tumal.”
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 Tokosra el fahk nu sel Ziba, “Ma nukewa su ma lal Mephibosheth, inge ma lom.” Ac Ziba el fahk, “Nga mwet kulansap lom, leum fulat luk, ac nga finsrak nga in akinsewowoye kom in pacl nukewa!”
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 Ke Tokosra David el sun acn Bahurim, sie mwet in sou lal Saul, su inel Shimei wen natul Gera, el illa in osun nu sel. El selngawel David ke el fahsr.
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 Shimei el mutawauk tanglal David ac mwet pwapa lal ah, David el ne kuhlusyukla ke mwet lal ac mwet mweun karinginyal.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 Shimei el selngawel ac fahk, “Tiok! Fahsrot! Kom mwet akmas! Kom mwet koluk!
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 Kom eisla tokosrai lal Saul, ac inge LEUM GOD El kai kom mweyen kom uniya mwet pukanten in sou lal Saul. LEUM GOD El sang tokosrai nu sel Absalom, wen nutum. Inge wanginla sripom, mweyen kom sie mwet akmas!”
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Abishai, su nina kial pa Zeruiah, el fahk nu sel tokosra, “Leum luk, efu kom ku lela kosro ngalngul soko ingan in selngawi kom? Lela ngan fahla pakela sifal!”
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 Tokosra el fahk nu sel Abishai ac Joab, tamulel lal, “Wangin ma lomtal ke ma se inge. El fin selngawiyu mweyen LEUM GOD El sap elan oru, na su ku in siyuk lah efu ku el oru?”
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 Ac David el fahk nu sel Abishai ac mwet pwapa nukewa lal, “Wen nutik sifacna el srike elan uniyuwi, na efu kowos ku lut ke mwet Benjamin se inge? LEUM GOD El fahk tuh elan selnga, na pa lela elan oru.
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 Sahp LEUM GOD El ac liye keok luk, ac ase kutu mwe insewowo in sang aol kas in selnga lal uh.”
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 Ouinge David ac mwet lal elos sifil fahsr inkanek lalos. Shimei el ukwalos na fahsr, tuh el ut pe eol uh. El fahsr na selngawelos ac tanglalos ke eot ac fohk.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 Tokosra ac mwet lal nukewa arulana totola ke elos sun Infacl Jordan, na elos mongla we.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 Absalom ac mwet Israel nukewa ma welul elos utyak nu Jerusalem, ac Ahithophel el welulos.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 Ke Hushai, kawuk se su David el lulalfongi, el osun nu sel Absalom, el wowoyak ac fahk, “In paht moul lal tokosra! In paht moul lal tokosra!”
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 Na Absalom el siyuk sel, “Mea sis kom tila insese nu sel David, mwet kawuk lom? Efu ku kom tia welul?”
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 Hushai el topuk, “Nga ac welul fuka? Nga ac wi na mwet se su suleyukla sin LEUM GOD ac sin mwet inge ac mwet Israel nukewa. Nga ac wi kom na.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 Ku su win ngan orekma nu se, fin tia wen nutin leum luk uh? Inge, nga fah kulansupwekom oana nga tuh kulansupu papa tomom meet.”
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 Na Absalom el forang nu sel Ahithophel ac siyuk sel, “Inge ke kut sun acn inge, mea kom nunku mu fal kut in oru?”
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 Na Ahithophel el fahk, “Fahla orek kosro nu sin mutan kulansap kien papa tomom, su el tuh filiya in liyaung lohm sin tokosra. Na mwet Israel nukewa ac fah etu lah papa tomom el nunku keim oana sie mwet lokoalok lal, ac ma se inge ac fah arulana akkeye insien mwet su fahsr tukum inge.”
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Ouinge elos tulokunak sie lohm nuknuk nu sel Absalom fin lohm sin tokosra. Na mwet nukewa liye na ke Absalom el utyak ac orek kosro nu sin mutan kulansap kien papa tumal ah.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 Kas in kasru nukewa su tuku sel Ahithophel in len ingo, mwet uh insese nu kac oana in ma tuku sin God me. David ac Absalom eltal tukeni na fahsr kac.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

< Luo Samuel 16 >