< Luo Samuel 10 >

1 Kutu pacl tok, Tokosra Nahash lun Ammon el misa, ac Hanun wen natul, el tokosrala.
Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Tokosra David el fahk, “Nga enenu in akkalemye nunak in kawuk pwaye luk nu sel Hanun, oana ke Nahash papa tumal, el tuh oru nu sik.” Ouinge David el supwala mwet utuk kas in fahkak nunak in pakomuta lal ke misa papa tumal ah. Ke elos sun acn Ammon,
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
3 mwet kol lun mwet Ammon elos fahk nu sin tokosra, “Ku kom nunku mu David el akfulatye papa tomom, pa sis el supwama mwet inge in fahkak kas in pakomuta lal nu sum? Sutuu na sutuu! El supwaltalma in tuh tuni siti uh, elan mau ku in eisla sesr!”
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Na Hanun el sruokya mwet utuk kas lal David, ac resaela alut lalos, ac wotela nuknuk lalos ah ke finyepalos, ac supwalosla.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
5 Elos arulana mwekin in folokla nu yen selos. Ke David el lohng ke ma sikyak ah, el sapla nu yorolos tuh elos in mutana Jericho ac tia foloko nwe ke alut lalos ah kapak.
Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Ke mwet Ammon elos akilen lah elos sifacna oru tuh David elan mwet lokoalokla lalos, na elos som moli longoul tausin mwet mweun Syria in acn Bethrehob ac Zobah, ac singoul luo tausin mwet Tob, oayapa tokosra lun Maacah wi sie tausin mwet.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
7 David el lohngak, na el supwalla Joab ac un mwet mweun lal nukewa.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
8 Mwet Ammon elos fahsr som nu ke nien utyak nu Rabbah, siti fulat lalos, ac tu na akola we. Mwet nukewa saya — mwet Syria, mwet Tob, ac mwet Maacah — elos som nu yen turangang ac akola pac in mweun we.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
9 Joab el liye tuh mwet lokoalok lalos ac mweunelos meet ah me ac tokolos me. Ouinge el sulela mwet ma wo emeet ke mweun sin mwet Israel, ac oakelosi in lain mwet Syria.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
10 Ac el sang Abishai, tamulel lal, in kol mwet mweun lula nukewa, na Abishai el oakelosi in lain mwet Ammon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
11 Joab el fahk nu sel, “Kom fin liye tuh mwet Syria ac kutangyula, na kom tuku kasreyu. Ac nga fin liye tuh mwet Ammon ac kutangkomla, na nga ac fahsrot kasrekom.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
12 Kom in ku ac pulaik! Lela kut in sang kuiyasr nufon in mweun ke mwet lasr ac ke siti nukewa lun God lasr. Finsrak tuh in fahsr ou ma lungse lun LEUM GOD!”
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
13 Joab ac mwet lal elos fahsryak nu ke mweun, ac mwet Syria elos kaing.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
14 Ke mwet Ammon elos liye lah mwet Syria kaing, na elos kaingla lukel Abishai, ac foloki nu in siti uh. Na Joab el forla sisla mweun lal yurin mwet Ammon, ac folokla nu Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
15 Mwet Syria elos akilen lah mwet Israel elos kutangulosla, na elos pangoneni mwet mweun lalos nukewa nu sie.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
16 Tokosra Hadadezer el sapla nu sin mwet Syria su muta layen kutulap in Infacl Euphrates, ac elos tuku nu Helam, ye kolyuk lal Shobach, captain lun un mwet mweun lal Tokosra Hadadezer lun Zobah.
Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
17 Ke David el lohngak ma inge, el orani mwet mweun lun Israel ac tupalla Infacl Jordan ac som nu Helam, yen mwet Syria elos akola soanel we. Mweun uh mutawauk,
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
18 na mwet Israel elos ukwauk mwet mweun Syria. David ac mwet lal ah uniya mwet itfoko su kasrusr ke chariot, ac angngaul tausin mwet kasrusr fin horse, ac elos kantelya Shobach, captain lun un mwet mweun su lainulos, ac el misa na yen mweun ah orek we.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
19 Ke tokosra ekasr su fahsr tokol Hadadezer elos akilen lah kutangyukla elos, na elos orek misla yurin mwet Israel, ac mutawauk orekma nu selos. Ac mwet Syria elos sangeng in sifilpa kasru mwet Ammon.
Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< Luo Samuel 10 >