< Luo Samuel 1 >

1 Tukun Saul el misa, David el foloko ke el tuh kutangla mwet Amalek, na el muta in acn Ziklag ke len luo.
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Ke len toko ah, mwet fusr se tuku liki nien aktuktuk lal Saul. El tuh seya nuknuk lal ac sang fohkfok nu fin sifal in akkalemye asor lal. El som nu yorol David ac srimi nwe infohk uh in akfulatyal.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 David el siyuk sel, “Kom tuku ya me?” El topuk, “Nga kaingla liki nien aktuktuk lun mwet Israel.”
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 David el fahk, “Fahk nu sik lah mea sikyak.” Na el topuk, “Mwet mweun lasr ah kaingla liki mweun ah, ac pukanten mwet lasr anwuki. Saul ac Jonathan wen natul, wi pac misa.”
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 Na David el fahk, “Kom etu fuka lah Saul ac Jonathan misa?”
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 El topuk, “Nga tuh muta Fineol Gilboa, ac nga liye ke Saul el fungyang nu fin osra natul ah, na chariot ac mwet kasrusr fin horse lun mwet lokoalok ah apkuranyang nu yorol.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Na el forma twe liyeyuyak, ac el pangonyu. Na nga fahk, ‘Mea?’
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Na el siyuk lah su nga uh, na nga fahk lah nga mwet Amalek.
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 Na el fahk, ‘Fahsru ac uniyuwi! Nga arulana kineta, ac nga apkuran in misa.’
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 Ouinge nga kalukyang nu yorol ac unilya, mweyen nga etu lah el ac na misa na el fin putatyang nu fac. Na nga eisla tefuro lal liki sifal, ac mwe naweyuk ke paol, pa nga use nu sum inge.”
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 David el arulana asor ac seya nuknuk lal, ac mwet lal nukewa oru oapana.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 Elos asor ac tung ac eoksra nwe ke ekela kacl Saul ac Jonathan, oayapa ke Israel, mwet lun LEUM GOD, mweyen arulana pukanten mwet anwuki ke mweun ah.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 Na David el siyuk sin mwet fusr se su use pweng se inge nu sel, “Kom mwet ya?” El topuk, “Nga mwet Amalek, tusruktu nga muta facl sum uh.”
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 David el siyuk sel, “Kom ku tia sangeng in uniya tokosra se su sulosolla sin LEUM GOD?”
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Na David el pangonma sie mwet lal ac fahk, “Unilya!” Ac mwet sac sringilya mwet Amalek sac, ac el misa.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 Ac David el fahk nu sin mwet Amalek sac, “Misa lom ma sum sifacna. Kom sifacna sot mwatum ke kom fahkak lah pwaye kom uniya sie su LEUM GOD El sulela in tokosra.”
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 David el onkakin on in eoksra se inge kacl Saul ac Jonathan,
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 ac el sapkin in lutiyuk nu sin mwet Judah. (Simla tari in [Book in Jashar].)
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 “Fin tohktok lun Israel, mwet kol lasr misa we! Mwet mweun pulaiklana lasr elos ikori we!
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Nimet fahkak nu in acn Gath, Ku ke inkanek in Ashkelon. Nimet oru tuh mutan Philistia in pwar; Nimet lela tuh an nutin mwet pegan in enganak.
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 “Lela in wangin af ku aunfong putat nu fin tohktok Gilboa; Lela in wangin fokin ima we pacl nukewa! Mwe mwekin se lah mwe loang lun mwet pulaik lasr in oan we; Mwe loang lal Saul tia sifil mosrweyuk.
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 Pisr natul Jonathan uniya mwet lokoalok puspis, Osra natul Saul tia etu pakoten — Sringilya mwet fokoko, ac uniya mwet lokoalok.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 “Saul ac Jonathan, wolana ac saok; Tukeni ke moul, tukeni ke misa; Mui liki eagle, fokoko liki lion.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 “Mutan Israel, kowos in mwemelil kacl Saul! El nukumkowosyang ke nuknuk srusra yohk molo, Ac nawekowos ke mwe yun ac gold.
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 “Mwet mweun pulaik ikori tari, Anwuki elos ke mweun. Jonathan el misa oan fin tohktok uh.
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 “Nga arulana asor keim, Jonathan, ma lik; Kom tuh arulana saok sik! Fuka lupan woiyen lungse lom nu sik, Wo liki lungse lun sie mutan.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 “Mwet mweun pulaik ikori tari, Mwe mweun natulos sisila ac wanginla sripa.”
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< Luo Samuel 1 >