< Luo Chronicle 5 >

1 Ke Tokosra Solomon el aksafyela orekma nukewa ke Tempul, el filiya ma nukewa ma David, papa tumal, el tuh kisakunla nu sin LEUM GOD (silver, gold, ac ma pac saya) tuh in oan in nien filma in Tempul.
Pamene ntchito yonse imene Solomoni anagwira pa Nyumba ya Yehova inatha, anabwera ndi zinthu zonse zimene abambo ake Davide anazipereka; siliva, golide ndi ziwiya. Anaziyika mʼzipinda zosungiramo chuma cha ku Nyumba ya Mulungu.
2 Na Tokosra Solomon el pangon mwet kol nukewa lun sruf ac sou lulap lun Israel tuh elos in tukeni nu Jerusalem, tuh elos in us Tuptup in Wuleang lun LEUM GOD liki Zion, Siti sel David, nu in Tempul.
Kenaka Solomoni anasonkhanitsa akuluakulu a Israeli mu Yerusalemu, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, mzinda wa Davide.
3 Elos nukewa fahsreni ke pacl in Kufwen lwen Aktuktuk.
Ndipo Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa mfumu nthawi ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
4 Ke pacl se mwet kol nukewa fahsreni, na mwet Levi elos srukak Tuptup in Wuleang,
Akuluakulu onse a Israeli atafika, Alevi ananyamula Bokosi la Chipangano,
5 ac us nu ke Tempul. Mwet tol ac mwet Levi elos oayapa moklela Lohm Nuknuk Mutal sin LEUM GOD ac ma nukewa kac, nu ke Tempul uh.
ndipo anabwera nalo bokosi lija pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula,
6 Tokosra Solomon ac mwet Israel nukewa elos toeni sisken na Tuptup in Wuleang, ac elos kisakin sheep ac cow na pukanten su kofla in oaoala.
ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.
7 Na mwet tol elos us Tuptup in Wuleang lun LEUM GOD nu in Tempul, ac likiya in Acn Mutal Na Mutal, ye cherub luo.
Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a Akerubi.
8 Posohksok lalos asrosrla ac afinya Tuptup sac oayapa sak usyen Tuptup sac.
Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira.
9 Pukun sak inge ku in liyeyuk mwet se fin tu suwohs nu kac ke mutun Acn Mutal Na Mutal, tuh tia ku in liyeyuk ke kutena acn saya. (Sak inge srakna oasr we nwe misenge.)
Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika, koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino.
10 Wangin kutena ma in Tuptup in Wuleang sac sayen eot sim luo ma Moses el tuh filiya loac Fineol Sinai, ke LEUM GOD El tuh orala wuleang yurin mwet Israel ke elos tuku liki acn Egypt.
Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
11 Ke mwet tol elos illa liki acn mutal uh (mwet tol nukewa su oasr in acn sac elos tuh akmutalyalos sifacna, mansis u se su lalos,
Kenaka ansembe anatulukamo mʼMalo Opatulika. Ansembe onse amene anali mʼmenemo anali atadziyeretsa posayangʼaniranso magulu awo ochokera.
12 ac mwet on nukewa lun mwet Levi — Asaph, Heman, Jeduthun, ac wen natulos ac sou lalos — los nukewa nukum nuknuk linen. Mwet Levi elos tu apkuran nu ke layen kutulap in loang sac, wi cymbal ac harp natulos, ac oayapa wi mwet tol siofok longoul su uk mwe ukuk.)
Alevi onse amene anali oyimba: Asafu, Hemani, Yedutuni ndi ana ndiponso abale awo, amayima mbali ya kummawa kwa guwa lansembe atavala zovala zofewa zosalala akuyimba ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe. Ansembe onse amene amayimba malipenga analipo 120 pamodzi.
13 Mwet on elos tukeni ke pusra sifanna in kaksakin ac sang kulo nu sin LEUM GOD. Ac ke pusren on uh ngisyak, wi pusren mwe ukuk ac cymbal ac kutu pac kain in mwe on, elos on ac fahk: “Kaksakin LEUM GOD mweyen El wo, Ac lungse lal oan ma pahtpat,” na lohm sac, lohm sin LEUM GOD, sessesla ke sie pukunyeng.
Oyimba malipenga ndi oyimba nyimbo aja amayimba mogwirizana, monga liwu la munthu mmodzi, kutamanda ndi kuyamika Yehova. Mogwirizana ndi malipenga, ziwaya zamalipenga ndi zida zina, anakweza mawu awo motamanda Yehova poyimba kuti, “Yehova ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.” Ndipo Nyumba ya Mulungu wa Yehova inadzaza ndi mtambo,
14 Ouinge mwet tol elos koflana tafwela alu lalos ke sripen pukunyeng sac, tuh wolana lun LEUM GOD nwakla in lohm sac.
choncho ansembe sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

< Luo Chronicle 5 >