< Luo Chronicle 26 >

1 Mwet Judah nukewa elos sulella Uzziah wen natul Amaziah, su yac singoul onkosr matwal, tuh elan tokosra in aol papa tumal ah.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 Tukun Amaziah el misa, Uzziah el sruokya siti Elath, ac sifilpa musaela.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Uzziah el tokosrala ke el yac singoul onkosr, ac el leum in Jerusalem ke yac lumngaul luo. Nina kial pa Jecoliah, sie mutan Jerusalem.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 El fahsr tukun ouiya lun papa tumal, ac oru ma su akinsewowoye LEUM GOD.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 Ke lusen na moul lal Zechariah, su luti nu sel tuh elan etu in sangeng sin God, Uzziah el oaru na in kulansupu LEUM GOD, ac God El akinsewowoyal.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Uzziah el som mweuni mwet Philistia. El kunausya pot in siti lun Gath, Jamnia, ac Ashdod, ac el musaela ac kuhlasak kutu siti apkuran nu Ashdod, ac oayapa in acn saya lun Philistia.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 God El kasrel in kutangla mwet Philistia, mwet Arab ma muta Gurbaal, ac mwet Meunim.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 Mwet Ammon elos sang takma nu sel Uzziah, pwanang el arulana kui, ac pweng kacl som nwe ke sun acn Egypt.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 Uzziah el musaela kais sie tower ke Mutunpot In Sruwasrik, ke Mutunpot Infahlfal, ac ke yen ma pot uh kuhfla we, in akkeyala pot ke acn Jerusalem.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 El oayapa musaela tower ke yen mwesis ac kuhlasak ke pot, ac el pukanak lufin kof pukanten, mweyen pukanten un kosro natul pe eol ac in acn tupasrpasr layen nu roto. Ke sripen el lungse orekma ke ima, el akkeye mwet uh in yoki ima in grape fin acn tohktok uh, ac orek ima yenwo fohk we.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Oasr un mwet mweun na yohk se lal su akola nu ke mweun. Ma simusla ke mwet mweun inge karinginyuk sel Jeiel ac Maaseiah, mwet sim luo lal su orekma ye kolyuk lal Hananiah, sie sin mwet pwapa lun tokosra.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 Mwet mweun lal uh kolyuk sin mwet kol luo tausin onfoko.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 Oasr mwet mweun tolfoko itkosr tausin lumfoko su akola in mweun kacl tokosra in lain mwet lokoalok lal.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 Uzziah el sang kufwen mweun nu sin mwet mweun inge, ke mwe loeyuk, osra in fahkfuk, mwe susu, nuknuk in mweun osra, pisr ac sukan pisr, oayapa eot nu ke fuht.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 Mwet usrnguk in kinauk ma sasu elos muta Jerusalem ac orala kufwen mwe pisr, oayapa mwe sis eot lulap liki tower ac liki sruwasrik ke pot in siti uh. Pweng kacl Uzziah fahsrelik nu yen nukewa, ac el arulana kui ke sripen kasru lun God nu sel.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 Tusruktu ke Tokosra Uzziah el mutawauk in kui, na el inse fulatyak, ac ma inge kololla nu ke musalla. El aklusrontenye LEUM GOD lal ke el som nu in Tempul ac sifacna akosak mwe keng fin loang lun mwe kisa keng.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 Azariah, mwet tol, ac mwet tol ku ac pulaik oalngoul sayal, welul utyak tokol tokosra
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 in kutongol, ac elos fahk nu sel, “Uzziah! Wangin suwohs lom in akosak mwe keng nu sin LEUM GOD. Mwet tol in fita lal Aaron mukena pa akmutalyeyukla in oru ma inge. Fahla liki acn mutal se inge. Kom oru ma koluk lain LEUM GOD, ke ma inge El ac fah tia sifil akinsewowoye kom.”
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Uzziah el srakna tu sisken loang sac in Tempul, ac sruok mwe neinyuk mwe keng se. El kasrkusrakak sin mwet tol inge, ac in kitin pacl ah na musen lepa sikyak ke motonsrol.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 Azariah ac mwet tol wial elos suiya motonsrol tokosra ac arulana lut, na elos lusulla liki Tempul. El sulaklak na illa mweyen LEUM GOD El kalyael.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 In pacl sac lac nwe ke el misa, tokosra el tia ku in sifil utyak nu in Tempul ke sripen mas se lal inge. Ke ma inge el srengla mutana in lohm sel sifacna, ac itukyang nu sel Jotham, wen natul, elan kol mutunfacl sac.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Mwet palu Isaiah wen natul Amoz, el simusla ma nukewa ma Tokosra Uzziah el orala ke pacl in leum lal ah.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 Uzziah el misa, ac pukpuki ke acn lun leum, tuh ke sripen mas lal ah el tia pukpuki inkulyuk lun mwet leum. Jotham, wen natul, el aolul in tokosra.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Luo Chronicle 26 >