< Luo Chronicle 24 >

1 Joash el mutawauk in tokosra fin acn Judah ke el yac itkosr, ac el leum in Jerusalem ke yac angngaul. Nina kial ah pa Zibiah, sie mutan Beersheba.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Joash el oru mwe insewowo nu sin LEUM GOD in pacl Jehoiada, mwet tol, el moul.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 Jehoiada el sulela mutan luo kial Tokosra Joash, ac eltal oswela wen ac acn nu sel.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 Tukun el tokosrala ke kutu yac, Joash el nunkauk in akwoyela Tempul.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 El sap mwet tol ac mwet Levi in som nu in siti nukewa lun Judah, ac orani lupan mani sin mwet uh ma ac fal in akwoyela acn ma musalla ke Tempul ke yac sac. El fahk mu elos in oru in sa, tuh pa mwet Levi inge pahtlac.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 Na el pangnolma Jehoiada, mwet kol lalos, ac multikin nu sel ac fahk, “Efu ku kom tia taran mwet Levi ingan in orani mani in tax sin mwet Judah ac Jerusalem, in oana ma Moses, mwet kulansap lun LEUM GOD, el tuh oakiya mwet uh in moli in sang kasru Lohm Nuknuk Mutal sin LEUM GOD
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 Mwet ma welulla Athaliah, mutan koluk sac, elos tuh aktaekyala Tempul, ac orekmakin kutu ma mutal we nu ke alu lalos nu sin Baal.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 Tokosra el sap mwet Levi in orala sie box in sang, ac filiya ke mutunoa in Tempul.
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 Elos supwalik kas nu in acn nukewa in Jerusalem ac Judah, tuh kais sie mwet in use tax lalos, oana ma Moses, mwet kulansap lun LEUM GOD, el tuh mutawauk oru yen mwesis.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 Mwet uh, oayapa mwet kol lalos, elos insewowo ke ma se inge, ac elos usani tax lalos ac nwakla box sac.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 Len nukewa mwet Levi elos ac usla box sac nu sin mwet roso lun tokosra su liyaung box sac. Fin sessesla, na mwet sim lun tokosra ac sie mwet aolyen mwet Tol Fulat ac usla ac okoala mani uh, na sifil folokunla box sac nu yen oan we uh. Ouinge lupan mani na yohk se ac orekeni.
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 Tokosra ac Jehoiada ac sang mani inge nu sin mwet kol orekma ke Tempul, ac elos ac sang moli mwet tufahl eot, mwet kamtu, ac mwet orekma pac ke osra, tuh elos in sang orala kutena acn musalla ke Tempul.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 Mwet nukewa moniyuk na in orekma, ac elos akwoyela Tempul arulana ku, oana ke tufahna orekla ah.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 Ke pacl se tari orekma sac, ma lula ke gold ac silver itukyang nu sin tokosra ac Jehoiada, ac eltal sang ma inge orala ahlu ku kutu pac mwe orekmak ma ac eneneyuk nu ke Tempul. Ke lusen pacl Jehoiada el moul, kisa uh orek in Tempul fal nu ke pacl la.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 Tukun el arulana matu ac sun yac siofok tolngoul, na el misa.
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 Elos piknilya inkulyuk lun mwet leum in Siti sel David, in asmakin orekma wo el oru nu sin mwet Israel, nu sin God, ac nu ke Tempul.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 Tusruktu tukunna Jehoiada el misa, mwet kol lun Judah elos kifasulla Tokosra Joash elan wela pwapa lalos uh.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 Ouinge mwet uh tia sifil alu in Tempul lun LEUM GOD, su God lun papa tumalos, a elos mutawauk alu nu ke ma sruloala kacl god mutan Asherah ac ma sruloala pac saya. Mwatalos ke ma koluk lalos inge pa pwanang kasrkusrak lun LEUM GOD tuku nu fin acn Judah ac Jerusalem.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 LEUM GOD El supwala mwet palu in akesmakinyalos elos in forla nu sel, a mwet uh srunga lohng.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 Na ngun lun God tuku nu facl Zechariah, wen natul Jehoiada mwet tol. El tu yen mwet uh ku in liyal we, ac wowoyak ac fahk, “LEUM GOD El siyuk lah efu ku kowos tia akos ma El sapkin, ac kowos use mwe ongoiya nu fowos sifacna! Kowos sisella, na pa El siskowosla!”
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 Tokosra Joash el weak mwet uh in lainul Zechariah, ac ke sap lal tokosra, mwet uh tanglal Zechariah ke nien tukeni inkul lun Tempul.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 Tokosra el mulkunla orekma kulang ma Jehoiada, papa tumal Zechariah, el tuh oru nu sel, ac el sap anwuki Zechariah. Meet liki na Zechariah el ac misa, el wola ac fahk, “Lela LEUM GOD Elan liye ma kom oru an, ac kalyei kom!”
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 Ke apkuran in safla yac sac, mwet mweun lun Syria mweuni acn Judah ac Jerusalem. Elos uniya mwet kol nukewa, ac usla ma wap puspis ke elos folokla nu Damascus.
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 Mwet mweun lun Syria tia pus, tusruktu LEUM GOD El sang kutangla nu selos fin mwet mweun pus lun Judah, mweyen mwet Judah elos ngetla liki LEUM GOD lun papa tumalos. Pa inge kaiyuk ma orek nu sel Tokosra Joash.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 El arulana kinetneta, ac ke mwet lokoalok lal som tari, na luo sin mwet pwapa lal sifacna eltal orek pwapa sulallal, ac unilya fin mwe oan kial, in aol ke el tuh akmuseya wen natul Jehoiada, mwet tol. Pukpuki el in Siti sel David, tusruktu tia ke inkulyuk lun mwet leum.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Mwet ma pwapa sulal ac unilya inge pa Zabad, wen nutin mutan Ammon se pangpang Shimeath, ac Jehozabad, wen nutin mutan Moab se pangpang Shimrith.
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 Sramsram ke mukul natul Joash, ac kas in palu lainul, oayapa ma simla ke orekma lal in akwoyela Tempul, oasr in [Book in Akkalemye Koanon Book In Tokosra]. Amaziah, wen natul, pa aolul in tokosra.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Luo Chronicle 24 >