< Sie Samuel 30 >

1 Tukun len luo, David ac mwet lal elos sun acn Ziklag. Mwet Amalek elos mweuni acn eir in acn Judah, ac elos utyak tari nu Ziklag. Elos esukak acn we,
Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
2 ac sruokya mutan nukewa. Elos tia uniya kutena mwet, tusruk elos usla mwet nukewa welulos ke elos som liki acn we.
Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
3 Ke David ac mwet lal tuku, elos liye tuh na siti sac firiryak, na sruhu ac utukla mutan kialos ac tulik natulos, mukul ac mutan.
Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
4 David ac mwet lal elos mutawauk in tung, ac elos tung nwe mas na.
Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
5 Finne Ahinoam ac Abigail, su eltal mutan kial David, elos utukla pac.
Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
6 David el muta in fosrnga lulap, mweyen mwet lal elos toasr na pwaye lah utukla tulik natulos, pwanang elos oru elos in tanglal David. Tusruktu David el ngetak nu sin LEUM GOD tuh Elan akkeyal.
Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
7 David el fahk nu sin mwet tol Abiathar, wen natul Ahimelech, “Use nuknuk ephod lun mwet tol,” na Abiathar el use ac sang nu sel.
Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
8 Na David el siyuk sin LEUM GOD, “Ya fal nga in som ukwe mwet su aklokoalokye kut? Nga ac ku in sruokolosi?” Na LEUM GOD El topuk, “Aok, ukwalos! Kom ac fah sruokolosi, ac kom fah molela mwet ma sruhu.”
Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
9 Ouinge David ac mwet onfoko lal elos som in ukwalos, ac ke elos sun Infacl srisrik Besor, kutu selos mutana we.
Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
10 David ac mwet angfoko lal sifilpa som. Mwet luofoko saya elos arulana totola ac tia ku in wi tupalla Infacl soko ah, oru elos mutana tia wi som.
Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
11 Mwet ma welul David elos konauk tulik mukul Egypt se yen mwesis ah, na elos usalu nu yorol David. Elos sang kutu bread nal ac kof nimal,
Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
12 ac fig paola, ac tun in grape pao luo. Ke el mongo tari na el kui. El tuh tia mongo ku nim ke lusen len tolu.
Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
13 David el siyuk sel, “Ku su leum lom uh, ac kom mwet oya?” Tulik sac fahk nu sel, “Nga mwet Egypt. Nga mwet kohs lun sie mwet Amalek. Leum luk ah som likiyu len tolu lac pa inge, mweyen nga luman mas kutu.
Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
14 Kut tuh som mweuni acn lun mwet Chereth ma oan eir in acn Judah, oayapa acn lun mwet in sou lal Caleb, ac kut esukak pac acn Ziklag.”
Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
15 Na David el siyuk sel, “Kom ku in pwen kut nu yurin u se ingan?” Tulik sac topuk, “Aok, kom fin wulela nu sik ye mutun God lah kom ac tia uniyuwi, ku usyula nu yurin leum luk.”
Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
16 Ac el pwanul David nu yurin u se ma orek lokoalok. Mwet inge elos oalik acn se elos muta we ah. Elos mongo ac nimnim ac orek engan in akfulatye lah arulana pus ma elos sruokya in facl lun mwet Philistia ac Judah.
Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
17 Toang in len tok ah, David el mweun lainulos. El mweunelos nwe ke na ekela. Oasr mwet angfoko sroang nu fin camel natulos ac kaingla, a funu mwet nukewa saya uh elos tiana kaingla.
Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
18 David el molela mwet nukewa ac ma nukewa ma mwet Amalek elos tuh usla, wi mutan luo kial sifacna.
Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
19 Wangin ma tuhlac. David el folokonma tulik mukul ac tulik mutan nukewa nutin mwet lal ah, oayapa ma nukewa mwet Amalek elos tuh usla.
Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
20 El oayapa folokonma un sheep ac cow ma utukla. Mwet lal elos oru kosro inge fahsr meet lukelos, ac elos fahk, “Ma inge nukewa ma lal David!”
Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
21 Na David el folokla nu yurin mwet luofoko ma tuh mutana Infacl srisrik Besor ke sripen elos arulana munas ac kofla welul. Elos tuyak in osun nu sel ac mwet lal, ac David el paingulos ke kas kulang.
Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
22 Tusruktu, kutu mukul srangesroa ac lusrongten sin mwet ma welul David som ah, elos fahk, “Mwet inge tiana wi kut som, na pa kut ac tiana sang nu selos ma kut eis inge. Elos in eis mutan kialos ac tulik natulos, ac fahla liki kut.”
Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
23 A David el fahk, “Ma lik, kowos tia ku in oru ouinge nu ke ma LEUM GOD El ase nu sesr! El molikutla, ac El ase kutangla nu sesr fin mwet lokoalok lasr.
Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
24 Wanginna mwet ku in insese nu ke ma kowos fahk inge! Mwet nukewa in eis oana sie. Ip se lun mwet su muta taran ma lasr, ac fah oana ip se lun mwet ma som wi mweun.”
Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
25 David el oakiya ma sap se inge, ac mwet Israel elos fahsrna kac nwe misenge.
Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
26 Ke David el folokla nu Ziklag, el supwala kutu ma wap inge nu sin mwet kawuk lal, su mwet kol in acn Judah, wi kas inge, “Mwe lung nu suwos inge, ma kut eisla sin mwet lokoalok lun LEUM GOD.”
Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
27 El supu ma inge nu sin mwet su muta Bethel, ac mwet su muta Ramah su oan eir in Judah, ac nu sin mwet su muta Jattir,
Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
28 Aroer, Siphmoth, Eshtemoa,
Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
29 ac Racal; ac nu sin sou lal Jerahmeel, ac nu sin mwet Ken,
Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
30 ac nu sin mwet su muta in siti Hormah, Borashan, Athach,
a ku Horima, Borasani, Ataki,
31 ac Hebron. El supu ma inge nu in acn nukewa ma el, ac mwet lal, elos tuh fufahsryesr we.
Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.

< Sie Samuel 30 >