< Sie Tokosra 13 >

1 Ke sap lun LEUM GOD, sie mwet palu in acn Judah el som nu Bethel ac sun acn we ke Jeroboam el tu ke loang sac ac akola in kisakin mwe kisa lal.
Ndipo taonani, munthu wa Mulungu wochokera ku Yuda anapita ku Beteli molamulidwa ndi Yehova. Nthawi imeneyo nʼkuti Yeroboamu atayimirira pambali pa guwa akufukiza lubani.
2 In oana ma LEUM GOD El sapkin, mwet palu sac el fahkak kas in lain loang sac ac fahk, “O loang, loang, pa inge ma LEUM GOD El fahk: Sie tulik, su ac fah pangpang Josiah, el ac fah isusla in sou lal David. Mwet tol su kulansap ke nien alu lun mwet pegan ac orek kisa fom, Josiah el ac fah onelosi pac fom, oayapa el ac fah esukak srin mwet misa fom.”
Mneneriyo anatemberera guwalo mofuwula potsata mawu a Yehova nati: “Guwa iwe, guwa iwe! Yehova akuti, ‘Taonani mʼbanja la Davide mudzabadwa mwana dzina lake Yosiya. Pa iwe, iyeyo adzaperekapo ngati nsembe, ansembe otumikira ku malo achipembedzo amene tsopano akufukiza lubani pa iwe, ndipo pa iwe adzatenthapo mafupa a anthu.’”
3 A mwet palu sac tafwelana in fahk, “Loang se inge ac fah fokelik, ac apat kac ac sohkelik, na kowos fah etu lah LEUM GOD El kaskas ke oalik.”
Tsiku lomwelo munthu wa Mulungu uja anapereka chizindikiro ichi: “Chizindikiro chimene Yehova wanena ndi ichi: Taonani guwali lidzangʼambika pakati ndipo phulusa lili pamenepo lidzamwazika.”
4 Ke pacl se Tokosra Jeroboam el lohng ma inge el asroela paol ac srisrngiya mwet paclu sac, ac fahk, “Sruokilya!” In kitin pacl ah na paol tokosra efla, ac el kofla kotani.
Mfumu Yeroboamu atamva zimene munthu wa Mulungu ananena motemberera guwa lansembe ku Beteli, anatambasula dzanja lake ali ku guwako ndipo anati, “Mugwireni!” Koma dzanja limene anatambasula kuloza munthu wa Mulunguyo linawuma kuti gwaa, kotero kuti sanathenso kulibweza.
5 Loang sac fokelik, ac apat kac rakelik ac oaclik infohk uh oana ma mwet palu sac palye Inen LEUM GOD.
Nthawi yomweyo guwa lija linangʼambika pakati ndipo phulusa lake linamwazika molingana ndi chizindikiro chimene munthu wa Mulungu anapereka potsata mawu a Yehova.
6 Tokosra Jeroboam el fahk nu sin mwet palu sac, “Nunak munas, pre keik nu sin LEUM GOD lom, ac siyuk Elan akkeyala pouk!” Mwet palu sa el pre nu sin LEUM GOD, ac paol tokosra kwela.
Pamenepo mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Undipempherere kwa Yehova Mulungu wako kuti andikomere mtima ndipo undipempherere kuti dzanja langa lichire.” Choncho munthu wa Mulungu anapempha kwa Yehova, ndipo dzanja la mfumu linachiritsidwa nʼkukhala ngati momwe linalili kale.
7 Na tokosra el fahk nu sin mwet palu sac, “Fahsru wiyu mongo in lohm sik. Nga ac akfalye nu sum ke ma kom oru inge.”
Mfumu inati kwa munthu wa Mulunguyo, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya, ndipo ndidzakupatsa mphatso.”
8 Na mwet palu sac topuk, “Kom finne use tafu mwe kasrup lom an, nga ac tiana wi kom som, ku kang ac nim kutena ma yurum.
Koma munthu wa Mulunguyo anayankha mfumu kuti, “Ngakhale mutandipatsa theka la chuma chanu, sindingapite nanu, kapena kudya chakudya, kapenanso kumwa madzi kuno.
9 LEUM GOD El sapkin nu sik ngan tiana kang ku nim kutena ma, oayapa ngan tia folok ke innek soko nga ut kac tuku ah.”
Pakuti Yehova anandilamula kuti, ‘Usakadye chakudya kapena kumwa madzi kapena kubwerera podzera njira imene unayendamo kale.’”
10 Ouinge el som ke soko pacna inkanek, ac tia ke innek soko el tuku kac me.
Choncho munthu wa Mulunguyo anadzera njira ina ndipo sanatsate njira imene anayendamo pobwera ku Beteliko.
11 In pacl sac, oasr mwet palu matu se muta in acn Bethel. Wen natul eltal tuku nu yorol ac fahk nu sel ma mwet palu se lun Judah el oru in acn Bethel ke len sac, ac ma el tuh fahk nu sel Tokosra Jeroboam.
Tsono ku Beteli kunkakhala mneneri wina wokalamba. Mmodzi mwa ana ake anamufotokozera zonse zomwe munthu wa Mulungu anachita kumeneko tsiku limenelo. Anawuzanso abambo ake zimene ananena kwa mfumu.
12 Ac mwet palu matu sac siyuk seltal, “Inkanek ya el ut we ke el folokla?” Eltal srusrngaung inkanek soko ah.
Abambo awo aja anawafunsa kuti, “Kodi wadzera njira iti?” Ana akewo anamufotokozera njira imene munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo anadzera.
13 Na el sap eltal in akoela donkey natul ah, ac eltal orala, na el som.
Ndipo abambo aja anati kwa ana akewo, “Mangireni chishalo pa bulu.” Anawo atamangirira chishalo pa bulu, nkhalambayo inakwera buluyo
14 El ukwe mwet palu Judah sac, ac konalak ke el muta ye sak oak soko. Ac el siyuk sel, “Ku kom pa mwet palu se lun Judah?” Mwet palu sac topuk, “Aok, nga.”
ndipo inalondola munthu wa Mulunguyo. Inamupeza atakhala pansi pa mtengo wa thundu ndipo inamufunsa kuti, “Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene anabwera kuchokera ku Yuda?” Munthuyo anayankha kuti, “Inde, ndineyo.”
15 Mwet sac fahk, “Fahsru wiyu mongo lohm sik ah.”
Choncho mneneri wokalambayo anati kwa iye, “Tiye kwathu kuti ukadye chakudya.”
16 Ac mwet palu lun Judah el fahk, “Nga koflana wi kom nu in lohm sum, ku eis mwe kulang sum. Ac nga fah tia mongo ku nim kutena ma yurum in acn se inge,
Munthu wa Mulungu uja anati, “Sindingabwerere nanu kapena kudya chakudya kapenanso kumwa madzi kuno.
17 mweyen LEUM GOD El sapkin ngan tiana kang ku nim kutena ma, ac nga in tia folok ke inkanek soko nga ut we tuku.”
Pakuti ndawuzidwa ndi Yehova kuti, ‘Usadye chakudya kapena kumwa madzi kumeneko kapenanso kubwerera poyenda njira imene unayendamo popita.’”
18 Na mwet palu matu se lun Bethel el fahk nu sel, “Nga pac, nga mwet palu se oana kom, ac LEUM GOD El sap sie lipufan in fahk nu sik ngan eis kom in wiyu nu lohm sik ah, ac kite kom ke mwe mongo ac mwe nim.” Tusruktu mwet palu matu sac el kikiap nu sel.
Mneneri wokalambayo anayankha kuti, “Inenso ndine mneneri ngati iwe. Ndipo mngelo wa Yehova anayankhula nane mawu a Yehova kuti, ‘Kamubweze abwere ku nyumba yako kuti akadye chakudya ndi kumwa madzi.’” Koma anamunamiza.
19 Ouinge mwet palu lun Judah el wi mwet palu matu sac folokla, ac mongo yorol in lohm sel.
Choncho munthu wa Mulungu uja anabwerera naye ndipo anakadya ndi kumwa madzi mʼnyumba mwake.
20 Ke eltal muta ke tepu lal, kas lun LEUM GOD tuku nu sin mwet palu matu sac,
Ali pa tebulo, Yehova anayankhula ndi mneneri wokalambayo amene anamubweza munthu wa Mulunguyo.
21 ac el liksreni na fahk nu sin mwet palu lun Judah, “LEUM GOD El fahk lah kom seakos ac tia oru ma El sapkin nu sum.
Iye anafuwulira munthu wa Mulungu wochokera ku Yudayo kuti, “Yehova akuti, ‘Iwe wanyoza mawu a Yehova ndipo sunasunge lamulo limene Yehova Mulungu wako anakupatsa.
22 A kom tuh foloko ac mongo acn ma El wuli kom in tiana mongo we. Ke ma inge kom ac anwuki, ac monum ac fah tia pukpuki inkulyuk lun sou lom.”
Iwe wabwerera ndi kudya chakudya ndiponso kumwa madzi ku malo amene Iye anakuwuza kuti usadye chakudya kapena kumwa madzi. Choncho mtembo wako sadzawuyika mʼmanda a makolo ako.’”
23 Tukun eltal mongo tari, mwet palu matu sac akoela donkey natul ah nu sin mwet palu lun Judah,
Munthu wa Mulungu atatha kudya ndi kumwa, mneneri amene anamubweza uja anamangirira chishalo pa bulu wa munthu wa Mulunguyo.
24 na el sroang nu fac ac som. Ac ke el kasrusr inkanek uh, lion soko sonol ac unilya. Na manol oanna inkanek ah, ac donkey soko ac lion soko ah tu na kac.
Akupita, anakumana ndi mkango pa msewu ndipo unamupha, mtembo wake unagwera pansi pa msewu, bulu uja anayima pambali pake ndipo mkango unayima pafupi ndi mtembowo.
25 Oasr kutu mwet fahsryak in acn sacn, ac liye mano sac oanna inkanek ah, ac lion soko ah tu siska. Elos alukela ac som na nu Bethel, ac fahkak ma elos liye ah.
Ndipo taonani, anthu ena amene ankapita mu msewumo anaona mtembowo uli pansi potero, mkango utayima pa mbali pa mtembo uja ndipo anapita nakafotokozera anthu mu mzinda umene mumakhala mneneri wokalamba uja.
26 Ke mwet palu matu sac lohng ma fwack inge, el fahk, “Pa ingan mwet palu se ma tia akos ma LEUM GOD El sapkin, na pa LEUM GOD El supwala lion soko in sruokilya ac unilya, in oana ma LEUM GOD El fahk kac.”
Mneneri amene anamubweza mnzake ku njira uja atamva zimenezi, anati, “Ameneyo ndi munthu wa Mulungu amene wanyoza mawu a Yehova. Yehova wamupereka kwa mkango umene wamukhadzula ndi kumupha, monga momwe Yehova anamuchenjezera.”
27 Na el fahk nu sin wen natul, “Akoela donkey nutik.” Ac eltal akoela,
Mneneri wokalambayo anati kwa ana ake, “Mundimangire chishalo pa bulu,” ndipo anaterodi.
28 na el som ac konauk mano sac oan inkanek ah, ac donkey soko ac lion soko ah srakna tu siska. Lion soko ah tiana kangla mano sac, ku anwuk nu sin donkey soko ah.
Ndipo anapita, nakapezadi mtembo utagwera pansi mu msewu, bulu pamodzi ndi mkango atayima pambali pake. Koma mkangowo sunadye mtembowo kapena kukhadzula buluyo.
29 Mwet palu matu sac srukak mano sac nu fin donkey natul, ac folokunla nu Bethel in asor kac, ac pikinya.
Choncho mneneri wokalambayo anatenga mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nawuyika pa bulu, ndipo anabwera nawo ku mzinda kuti alire maliro ndi kuyika mtembowo mʼmanda.
30 El pikinya inkulyuk lun sou lal sifacna, na el ac wen natul asor kacl ac fahk, “O, ma lik, ma lik!”
Tsono anayika mtembowo mʼmanda amene mneneri wokalamba uja anadzikonzera, ndipo anamulira pomanena kuti, “Mʼbale wanga ine! Mʼbale wanga ine!”
31 Tukun pukpuki mwet sac, mwet palu matu sac fahk nu sin wen natul, “Nga fin misa, komtal pikinyuwi na inkulyuk se inge, ac filiyuwi siskal.
Atamuyika mʼmanda, iye anati kwa ana ake, “Ine ndikafa, mudzandiyike mʼmanda amene munthu wa Mulungu wayikidwa. Mudzayike mafupa anga pambali pa mafupa ake.
32 Kas ma el fahk lain loang se in acn Bethel, ac lain nien alu nukewa in siti srisrik in acn Samaria, oana ma LEUM GOD El sapkin, pwayena lah ma inge nukewa ac fah akpwayeyuk.”
Pakuti uthenga umene Yehova anamuyankhulitsa, wotsutsana ndi guwa lansembe la ku Beteli ndi nyumba zonse za chipembedzo za mʼmizinda ya ku Samariya, zidzachitika ndithu.”
33 Tokosra Jeroboam lun Israel el tiana forla liki ouiyen moul koluk lal, a el srakna sulela mwet tol lal sin kutena sou tuh elos in kulansap ke loang ma el musaela. Ac el mosrwela kutena mwet su lungse in mwet tol.
Ngakhale izi zinachitika, Yeroboamu sanasiye njira zake zoyipa, koma anasankhanso anthu wamba kukhala ansembe pa malo ake achipembedzo. Aliyense amene ankafuna kukhala wansembe iye anamupatula kukhala wansembe.
34 Ma koluk se lal inge pa kunausla mwet lal, ac ikruiya tokosrai lal.
Limeneli ndiye linali tchimo la nyumba ya Yeroboamu limene linabweretsa kugwa kwake ndiponso chiwonongeko mʼdzikomo.

< Sie Tokosra 13 >