< 시편 66 >

1 (시. 영장으로 한 노래) 온 땅이여, 하나님께 즐거운 소리를 발할지어다
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 그 이름의 영광을 찬양하고 영화롭게 찬송할지어다
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 하나님께 고하기를 주의 일이 어찌 그리 엄위하신지요 주의 큰 권능으로 인하여 주의 원수가 주께 복종할 것이며
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 온 땅이 주께 경배하고 주를 찬양하며 주의 이름을 찬양하리이다 할지어다 (셀라)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 와서 하나님의 행하신 것을 보라 인생에게 행하심이 엄위하시도다
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 하나님이 바다를 변하여 육지되게 하셨으므로 무리가 도보로 강을 통과하고 우리가 거기서 주로 인하여 기뻐하였도다
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 저가 그 능으로 영원히 치리하시며 눈으로 열방을 감찰하시나니 거역하는 자는 자고하지 말지어다 (셀라)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 만민들아! 우리 하나님을 송축하며 그 송축소리로 들리게 할찌어다
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 그는 우리 영혼을 살려 두시고 우리의 실족함을 허락지 아니하시는 주시로다
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 하나님이여, 주께서 우리를 시험하시되 우리를 단련하시기를 은을 단련함 같이 하셨으며
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 우리를 끌어 그물에 들게 하시며 어려운 짐을 우리 허리에 두셨으며
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 사람들로 우리 머리 위로 타고 가게 하셨나이다 우리가 불과 물을 통행하더니 주께서 우리를 끌어내사 풍부한 곳에 들이셨나이다
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 내가 번제를 가지고 주의 집에 들어가서 나의 서원을 갚으리니
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 이는 내 입술이 발한 것이요 내 환난 때에 내 입이 말한 것이니이다
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 내가 수양의 향기와 함께 살진 것으로 주께 번제를 드리며 수소와 염소를 드리리이다 (셀라)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 하나님을 두려워하는 너희들아 다 와서 들으라 하나님이 내 영혼을 위하여 행하신 일을 내가 선포하리로다
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 내가 내 입으로 그에게 부르짖으며 내 혀로 높이 찬송하였도다
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 내가 내 마음에 죄악을 품으면 주께서 듣지 아니하시리라
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 그러나 하나님이 실로 들으셨으며 내 기도 소리에 주의하셨도다
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 하나님을 찬송하리로다! 저가 내 기도를 물리치지 아니하시고 그 인자하심을 내게서 거두지도 아니하셨도다
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< 시편 66 >