< 시편 54 >
1 (다윗의 마스길. 영장으로 현악에 맞춘 노래. 십인이 사울에게 이르러 말하기를 다윗이 우리 곳에 숨지 아니하였나이까 하던 때에) 하나님이여, 주의 이름으로 나를 구원하시고 주의 힘으로 나를 판단하소서
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 하나님이여, 내 기도를 들으시며 내 입의 말에 귀를 기울이소서
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 외인이 일어나 나를 치며 강포한 자가 내 생명을 수색하며 하나님이 자기 앞에 두지 아니하였음이니이다 (셀라)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 하나님은 나의 돕는 자시라 주께서 내 생명을 붙드는 자와 함께 하시나이다
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 주께서 내 원수에게 악으로 갚으시리니 주의 성실하심으로 저희를 멸하소서
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 내가 낙헌제로 주께 제사하리이다 여호와여, 주의 이름에 감사하오리니 주의 이름이 선하심이니이다
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 대저 주께서 모든 환난에서 나를 건지시고 내 원수가 보응 받는 것을 나로 목도케 하셨나이다
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.