< 시편 25 >

1 (다윗의 시) 여호와여, 나의 영혼이 주를 우러러 보나이다
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 나의 하나님이여, 내가 주께 의지하였사오니 나로 부끄럽지 않게하시고 나의 원수로 나를 이기어 개가를 부르지 못하게 하소서
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 주를 바라는 자는 수치를 당하지 아니하려니와 무고히 속이는 자는 수치를 당하리이다
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 여호와여, 주의 도를 내게 보이시고 주의 길을 내게 가르치소서
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 주의 진리로 나를 지도하시고 교훈하소서 주는 내 구원의 하나님이시니 내가 종일 주를 바라나이다
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 여호와여, 주의 긍휼하심과 인자하심이 영원부터 있었사오니 주여, 이것을 기억하옵소서
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 여호와여, 내 소시의 죄와 허물을 기억지 마시고 주의 인자하심을 따라 나를 기억하시되 주의 선하심을 인하여 하옵소서
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 여호와는 선하시고 정직하시니 그러므로 그 도로 죄인을 교훈하시리로다
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 온유한 자를 공의로 지도하심이여 온유한 자에게 그 도를 가르치시리로다
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 여호와의 모든 길은 그 언약과 증거를 지키는 자에게 인자와 진리로다
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 여호와여, 나의 죄악이 중대하오니 주의 이름을 인하여 사하소서
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 여호와를 경외하는 자 누구뇨? 그 택할 길을 저에게 가르치시리로다
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 저의 영혼은 평안히 거하고 그 자손은 땅을 상속하리로다
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 여호와의 친밀함이 경외하는 자에게 있음이여 그 언약을 저희에게 보이시리로다
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 내 눈이 항상 여호와를 앙망함은 내 발을 그물에서 벗어나게 하실 것임이로다
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 주여, 나는 외롭고 괴롭사오니 내게 돌이키사 나를 긍휼히 여기소서
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 내 마음의 근심이 많사오니 나를 곤난에서 끌어 내소서
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 나의 곤고와 환난을 보시고 내 모든 죄를 사하소서
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 내 원수를 보소서 저희가 많고 나를 심히 미워함이니이다
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 내 영혼을 지켜 나를 구원하소서 내가 주께 피하오니 수치를 당치 말게 하소서
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 내가 주를 바라오니 성실과 정직으로 나를 보호하소서
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 하나님이여, 이스라엘을 그 모든 환난에서 구속하소서
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< 시편 25 >