< 시편 122 >
1 (다윗의 시. 곧 성전에 올라가는 노래) 사람이 내게 말하기를 여호와의 집에 올라가자 할 때에 내가 기뻐하였도다
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 예루살렘아! 우리 발이 네 성문 안에 섰도다
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 예루살렘아! 너는 조밀한 성읍과 같이 건설되었도다
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 지파들 곧 여호와의 이름에 감사하려고 이스라엘의 전례대로 그리로 올라가는도다
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 거기 판단의 보좌를 두셨으니 곧 다윗 집의 보좌로다
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 예루살렘을 위하여 평안을 구하라 예루살렘을 사랑하는 자는 형통하리로다
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 네 성 안에는 평강이 있고 네 궁중에는 형통이 있을지어다
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 내가 내 형제와 붕우를 위하여 이제 말하리니 네 가운데 평강이 있을지어다
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 여호와 우리 하나님의 집을 위하여 내가 네 복을 구하리로다
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.