< 시편 111 >

1 할렐루야! 내가 정직한 자의 회와 공회 중에서 전심으로 여호와께 감사하리로다
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 여호와의 행사가 크시니 이를 즐거워하는 자가 다 연구하는도다
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 그 행사가 존귀하고 엄위하며 그 의가 영원히 있도다
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 그 기이한 일을 사람으로 기억케 하셨으니 여호와는 은혜로우시고 자비하시도다
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 여호와께서 자기를 경외하는 자에게 양식을 주시며 그 언약을 영원히 기억하시리로다
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 저가 자기 백성에게 열방을 기업으로 주사 그 행사의 능을 저희에게 보이셨도다
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 그 손의 행사는 진실과 공의며 그 법도는 다 확실하니
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 영원 무궁히 정하신 바요 진실과 정의로 행하신 바로다
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 여호와께서 그 백성에게 구속을 베푸시며 그 언약을 영원히 세우셨으니 그 이름이 거룩하고 지존하시도다
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 여호와를 경외함이 곧 지혜의 근본이라 그 계명을 지키는 자는 다 좋은 지각이 있나니 여호와를 찬송함이 영원히 있으리로다
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< 시편 111 >