< 잠언 4 >

1 아들들아 아비의 훈계를 들으며 명철을 얻기에 주의하라
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 내가 선한 도리를 너희에게 전하노니 내 법을 떠나지 말라
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 나도 내 아버지에게 아들이었었으며 내 어머니 보기에 유약한 외아들이었었노라
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 아버지가 내게 가르쳐 이르기를 내 말을 네 마음에 두라 내 명령을 지키라 그리하면 살리라
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 지혜를 얻으며 명철을 얻으라 내 입의 말을 잊지 말며 어기지 말라
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 지혜를 버리지 말라 그가 너를 보호하리라 그를 사랑하라 그가 너를 지키리라
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 지혜가 제일이니 지혜를 얻으라! 무릇 너의 얻은 것을 가져 명철을 얻을지니라
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 그를 높이라 그리하면 그가 너를 높이 들리라 만일 그를 품으면 그가 너를 영화롭게 하리라
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 그가 아름다운 관을 네 머리에 두겠고 영화로운 면류관을 네게 주리라 하였느니라
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 내 아들아 들으라 내 말을 받으라! 그리하면 네 생명의 해가 길리라
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 내가 지혜로운 길로 네게 가르쳤으며 정직한 첩경으로 너를 인도하였은즉
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 다닐 때에 네 걸음이 곤란하지 아니하겠고 달려갈 때에 실족하지 아니하리라
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 훈계를 굳게 잡아 놓치지 말고 지키라 이것이 네 생명이니라
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 사특한 자의 첩경에 들어가지 말며 악인의 길로 다니지 말지어다
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 그 길을 피하고 지나가지 말며 돌이켜 떠나갈지어다
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 그들은 악을 행하지 못하면 자지 못하며 사람을 넘어뜨리지 못하면 잠이 오지 아니하며
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 불의의 떡을 먹으며 강포의 술을 마심이니라
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 의인의 길은 돋는 햇볕 같아서 점점 빛나서 원만한 광명에 이르거니와
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 악인의 길은 어둠 같아서 그가 거쳐 넘어져도 그것이 무엇인지 깨닫지 못하느니라
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 내 아들아 내 말에 주의하며 나의 이르는 것에 네 귀를 기울이라
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 그것을 네 눈에서 떠나게 말며 네 마음 속에 지키라
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 그것은 얻는 자에게 생명이 되며 그 온 육체의 건강이 됨이니라
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 무릇 지킬만한 것보다 더욱 네 마음을 지키라 생명의 근원이 이에서 남이니라
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 궤휼을 네 입에서 버리며 사곡을 네 입술에서 멀리하라
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 네 눈은 바로 보며 네 눈꺼풀은 네 앞을 곧게 살펴
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 네 발의 행할 첩경을 평탄케 하며 네 모든 길을 든든히 하라
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 우편으로나 좌편으로나 치우치지 말고 네 발을 악에서 떠나게 하라
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< 잠언 4 >