< 잠언 31 >
1 르무엘왕의 말씀한바 곧 그 어머니가 그를 훈계한 잠언이라
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 내 아들아 내가 무엇을 말할꼬 내 태에서 난 아들아 내가 무엇을 말할꼬 서원대로 얻은 아들아 내가 무엇을 말할꼬
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 네 힘을 여자들에게 쓰지 말며 왕들을 멸망시키는 일을 행치 말지어다
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 르무엘아 포도주를 마시는 것이 왕에게 마땅치 아니하고 왕에게 마땅치 아니하며 독주를 찾는 것이 주권자에게 마땅치 않도다
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 술을 마시다가 법을 잊어버리고 모든 간곤한 백성에게 공의를 굽게 할까 두려우니라
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 독주는 죽게된 자에게, 포도주는 마음에 근심하는 자에게 줄지어다
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 그는 마시고 빈궁한 것을 잊어버리겠고 다시 그 고통을 기억지 아니하리라
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 너는 벙어리와 고독한 자의 송사를 위하여 입을 열지니라
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 너는 입을 열어 공의로 재판하여 간곤한 자와 궁핍한 자를 신원할지니라
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 누가 현숙한 여인을 찾아 얻겠느냐 그 값은 진주보다 더 하니라
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 그런 자의 남편의 마음은 그를 믿나니 산업이 핍절치 아니하겠으며
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 그런 자는 살아 있는 동안에 그 남편에게 선을 행하고 악을 행치아니하느니라
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 그는 양털과 삼을 구하여 부지런히 손으로 일하며
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 상고의 배와 같아서 먼 데서 양식을 가져오며
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 밤이 새기 전에 일어나서 그 집 사람에게 식물을 나눠주며 여종에게 일을 정하여 맡기며
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 밭을 간품하여 사며 그 손으로 번 것을 가지고 포도원을 심으며
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 힘으로 허리를 묶으며 그 팔을 강하게 하며
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 자기의 무역하는 것이 이로운 줄을 깨닫고 밤에 등불을 끄지 아니하고
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 손으로 솜뭉치를 들고 손가락으로 가락을 잡으며
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 그는 간곤한 자에게 손을 펴며 궁핍한 자를 위하여 손을 내밀며
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 그 집 사람들은 다 홍색 옷을 입었으므로 눈이 와도 그는 집 사람을 위하여 두려워하지 아니하며
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 그는 자기를 위하여 아름다운 방석을 지으며 세마포와 자색 옷을 입으며
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 그 남편은 그 땅의 장로로 더불어 성문에 앉으며 사람의 아는 바가 되며
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 그는 베로 옷을 지어 팔며 띠를 만들어 상고에게 맡기며
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 입을 열어 지혜를 베풀며 그 혀로 인애의 법을 말하며
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 그 집안 일을 보살피고 게을리 얻은 양식을 먹지 아니하나니
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 그 자식들은 일어나 사례하며 그 남편은 칭찬하기를
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 덕행 있는 여자가 많으나 그대는 여러 여자보다 뛰어난다 하느니라
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 고운 것도 거짓되고 아름다운 것도 헛되나 오직 여호와를 경외하는 여자는 칭찬을 받을 것이라
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 그 손의 열매가 그에게로 돌아갈 것이요 그 행한 일을 인하여 성문에서 칭찬을 받으리라
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.