< 잠언 1 >

1 다윗의 아들 이스라엘 왕 솔로몬의 잠언이라
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 이는 지혜와 훈계를 알게 하며 명철의 말씀을 깨닫게 하며
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 지혜롭게, 의롭게, 공평하게, 정직하게, 행할 일에 대하여 훈계를 받게 하며
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 어리석은 자로 슬기롭게 하며 젊은 자에게 지식과 근신함을 주기 위한 것이니
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 지혜있는 자는 듣고 학식이 더할 것이요 명철한 자는 모략을 얻을 것이라
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 잠언과 비유와 지혜있는 자의 말과 그 오묘한 말을 깨달으리라
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 여호와를 경외하는 것이 지식의 근본이어늘 미련한 자는 지혜와 훈계를 멸시하느니라
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 내 아들아 네 아비의 훈계를 들으며 네 어미의 법을 떠나지 말라
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 이는 네 머리의 아름다운 관이요 네 목의 금사슬이니라
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 내 아들아 악한 자가 너를 꾈지라도 좇지 말라 내 아들아 악한 자가 너를 꾈지라도 좇지 말라
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 그들이 네게 말하기를 우리와 함께 가자 우리가 가만히 엎드렸다가 사람의 피를 흘리자 죄없는 자를 까닭없이 숨어 기다리다가
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 음부 같이 그들을 산 채로 삼키며 무덤에 내려가는 자 같게 통으로 삼키자 (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 우리가 온갖 보화를 얻으며 빼앗은 것으로 우리 집에 채우리니
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 너는 우리와 함께 제비를 뽑고 우리가 함께 전대 하나만 두자 할지라도
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 내 아들아 그들과 함께 길에 다니지 말라 네 발을 금하여 그 길을 밟지 말라
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 대저 그 발은 악으로 달려가며 피를 흘리는 데 빠름이니라
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 무릇 새가 그물 치는 것을 보면 헛 일이겠거늘
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 그들의 가만히 엎드림은 자기의 피를 흘릴 뿐이요 숨어 기다림은 자기의 생명을 해할 뿐이니
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 무릇 이를 탐하는 자의 길은 다 이러하여 자기의 생명을 잃게 하느니라
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 지혜가 길거리에서 부르며 광장에서 소리를 높이며
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 훤화하는 길 머리에서 소리를 지르며 성문 어귀와 성중에서 그 소리를 발하여 가로되
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 너희 어리석은 자들은 어리석음을 좋아하며 거만한 자들은 거만을 기뻐하며 미련한 자들은 지식을 미워하니 어느 때까지 하겠느냐
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 나의 책망을 듣고 돌이키라 보라 내가 나의 신을 너희에게 부어주며 나의 말을 너희에게 보이리라
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 내가 부를지라도 너희가 듣기 싫어 하였고 내가 손을 펼지라도 돌아보는 자가 없었고
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 도리어 나의 모든 교훈을 멸시하며 나의 책망을 받지 아니하였은즉
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 너희가 재앙을 만날 때에 내가 웃을 것이며 너희에게 두려움이 임할 때에 내가 비웃으리라
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 너희의 두려움이 광풍같이 임하겠고 너희의 재앙이 폭풍같이 임하리니
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 그 때에 너희가 나를 부르리라 그래도 내가 대답지 아니하겠고 부지런히 나를 찾으리라 그래도 나를 만나지 못하리니
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 대저 너희가 지식을 미워하며 여호와 경외하기를 즐거워하지 아니하며
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 나의 교훈을 받지 아니하고 나의 모든 책망을 업신여겼음이라
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 그러므로 자기 행위의 열매를 먹으며 자기 꾀에 배부르리라
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 어리석은 자의 퇴보는 자기를 죽이며 미련한 자의 안일은 자기를 멸망시키려니와
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 오직 나를 듣는 자는 안연히 살며 재앙의 두려움이 없이 평안하리라
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< 잠언 1 >