< 민수기 1 >

1 이스라엘 자손이 애굽 땅에서 나온 후 제 이년 이월 일일에 여호와께서 시내 광야 회막에서 모세에게 일러 가라사대
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 너희는 이스라엘 자손의 모든 회중 각 남자의 수를 그들의 가족과 종족을 따라 그 명수대로 계수할지니
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 이스라엘 중 이십세 이상으로 싸움에 나갈만한 모든 자를 너와 아론은 그 군대대로 계수하되
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 매 지파의 각기 종족의 두령 한 사람씩 너희와 함께 하라
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 너희와 함께 설 사람들의 이름은 이러하니 르우벤에게서는 스데울의 아들 엘리술이요
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 시므온에게서는 수리삿대의 아들 슬루미엘이요
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 유다에게서는 암미나답의 아들 나손이요
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 잇사갈에게서는 수리알의 아들 느다넬이요
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 스불론에게서는 헬론의 아들 엘리압이요
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 요셉 자손에게서는 에브라임에 암미훗의 아들 엘리사마와, 므낫세에 브다술의 아들 가말리엘이요
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 베냐민에게서는 기드오니의 아들 아비단이요
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 단에게서는 암미삿대의 아들 아히에셀이요
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 아셀에게서는 오그란의 아들 바기엘이요
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 갓에게서는 드우엘의 아들 엘리아삽이요
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 납달리에게서는 에난의 아들 아히라니라 하시니
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 그들은 회중에서 부름을 받은 자요 그 조상 지파의 족장으로서 이스라엘 천만인의 두령이라
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 모세와 아론이 지명된 이 사람들을 데리고
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 이월 일일에 온 회중을 모으니 그들이 각기 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 그 명수를 의지하여 자기 계통을 말하매
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 여호와께서 모세에게 명하신 대로 그가 시내 광야에서 그들을 계수하였더라
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 이스라엘의 장자 르우벤의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈만한 각 남자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 르우벤 지파의 계수함을 입은 자가 사만 육천 오백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 시드몬의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈만한 각 남자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 시므온 지파의 계수함을 입은 자가 오만 구천 삼백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 갓의 아들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 갓 지파의 계수함을 입은 자가 사만 오천 육백 오십명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 유다의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 유다 지파의 계수함을 입은자가 칠만 사천 육백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 잇사갈의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 잇사갈 지파의 계수함을 입은자가 오만 사천 사백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 스불론의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 스불론 지파의 계수함을 입은 자가 오만 칠천 사백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 요셉의 아들 에브라임의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 에브라임 지파의 계수함을 입은 자가 사만 오백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 므낫세의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 므낫세 지파의 계수함을 입은 자가 삼만 이천 이백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 베냐민의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 단의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 베냐민 지파의 계수함을 입은 자가 삼만 오천 사백명이었더라 단의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니 베냐민 지파의 계수함을 입은 자가 삼만 오천 사백명이었더라
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 단 지파의 계수함을 입은 자가 육만 이천 칠백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 아셀의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 아셀 지파의 계수함을 입은 자가 사만 일천 오백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 납달리의 아들들에게서 난 자를 그들의 가족과 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자를 그 명수대로 다 계수하니
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 납달리 지파의 계수함을 입은 자가 오만 삼천 사백명이었더라
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 이 계수함을 입은 자는 모세와 아론과 각기 이스라엘 종족을 대표한 족장 십 이인이 계수한 자라
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 이같이 이스라엘 자손의 그 종족을 따라 이십세 이상으로 싸움에 나갈 만한 자가 이스라엘 중에서 다 계수함을 입었으니
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 계수함을 입은 자의 총계가 육십만 삼천 오백 오십명이었더라
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 오직 레위인은 그 조상의 지파대로 그 계수에 들지 아니하였으니
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 이는 여호와께서 모세에게 일러 가라사대
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 레위 지파만은 너는 계수치 말며 그들을 이스라엘 자손 계수중에 넣지 말고
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 그들을 증거막과 그 모든 기구와 그 모든 부속품을 관리하게 하라
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 그들은 그 장막과 그 모든 기구를 운반하며 거기서 봉사하며 장막 사면에 진을 칠지며
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 장막을 운반할 때에는 레위인이 그것을 걷고 장막을 세울 때에는 레위인이 그것을 세울 것이요 외인이 가까이 오면 죽일지며
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 레위인은 증거막 사면에 진을 쳐서 이스라엘 자손의 회중에게 진노가 임하지 않게 할 것이라 레위인은 증거막에 대한 책임을 지킬지니라! 하셨음이라
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 이스라엘 자손이 그대로 행하되 여호와께서 모세에게 명하신 대로 행하였더라
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< 민수기 1 >