< 욥기 41 >

1 네가 능히 낚시로 악어를 낚을 수 있겠느냐 노끈으로 그 혀를 맬수 있겠느냐
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 줄로 그 코를 꿸 수 있겠느냐 갈고리로 그 아가미를 꿸 수 있겠느냐
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 그것이 어찌 네게 연속 간구하겠느냐 유순한 말로 네게 이야기하겠느냐
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 어찌 너와 계약하고 영영히 네 종이 되겠느냐
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 네가 어찌 새를 놀리는것 같이 그것을 놀리겠으며 네 소녀들을 위하여 그것을 매어 두겠느냐
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 어찌 어부의 떼가 그것으로 상품을 삼아 상고들 가운데 나눌 수 있겠느냐
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 네가 능히 창으로 그 가죽을 찌르거나 작살로 그 머리를 찌를 수 있겠느냐
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 손을 그것에게 좀 대어 보라 싸울 일이 생각나서 다시는 아니하리라
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 잡으려는 소망은 헛것이라 그것을 보기만 하여도 낙담하지 않겠느냐
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 아무도 그것을 격동시킬 용맹이 없거든 능히 나를 당할 자가 누구냐
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 누가 먼저 내게 주고 나로 갚게 하였느냐 온 천하에 있는 것이 다 내 것이니라
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 내가 악어의 지체와 큰 힘과 훌륭한 구조에 대하여 잠잠치 아니하리라
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 누가 그 가죽을 벗기겠으며 그 아가미 사이로 들어가겠는고
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 누가 그 얼굴의 문을 열 수 있을까 그 두루 있는 이가 두렵구나
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 견고한 비늘은 그의 자랑이라 서로 연함이 봉한 것 같구나
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 이것 저것이 한데 붙었으니 바람도 그 사이로 들어가지 못하겠고
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 서로 연하여 붙었으니 능히 나눌 수도 없구나
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 그것이 재채기를 한즉 광채가 발하고 그 눈은 새벽 눈꺼풀이 열림같으며
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 그 입에서는 횃불이 나오고 불똥이 뛰어나며
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 그 콧구멍에서는 연기가 나오니 마치 솥이 끓는 것과 갈대의 타는 것 같구나
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 그 숨이 능히 숯불을 피우니 불꽃이 그 입에서 나오며
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 힘이 그 목에 뭉키었고 두려움이 그 앞에서 뛰는구나
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 그 살의 조각들이 서로 연하고 그 몸에 견고하여 움직이지 아니하며
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 그 마음이 돌 같이 단단하니 그 단단함이 맷돌 아랫짝 같구나
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 그것이 일어나면 용사라도 두려워하며 경겁하여 창황하며
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 칼로 칠지라도 쓸데없고 창이나 살이나 작살도 소용이 없구나
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 그것이 철을 초개 같이, 놋을 썩은 나무 같이 여기니
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 살이라도 그것으로 도망하게 못하겠고 물매돌도 그것에게는 겨같이 여기우는구나
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 몽둥이도 검불 같이 보고 창을 던짐을 우습게 여기며
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 그 배 아래는 날카로운 와륵 같으니 진흙 위에 타작 기계 같이 자취를 내는구나
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 깊은 물로 솥의 물이 끓음 같게 하며 바다로 젖는 향기름 같게 하고
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 자기 뒤에 광채나는 길을 내니 사람의 보기에 바닷물이 백발 같구나
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 땅 위에는 그것 같은 것이 없나니 두려움 없게 지음을 받았음이라
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 모든 높은 것을 낮게 보고 모든 교만한 것의 왕이 되느니라
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< 욥기 41 >