< 욥기 38 >

1 때에 여호와께서 폭풍 가운데로서 욥에게 말씀하여 가라사대
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 무지한 말로 이치를 어둡게 하는 자가 누구냐
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 너는 대장부처럼 허리를 묶고 내가 네게 묻는 것을 대답할지니라
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 내가 땅의 기초를 놓을 때에 네가 어디 있었느냐 네가 깨달아 알았거든 말할지니라
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 누가 그 도량을 정하였었는지 누가 그 준승을 그 위에 띄웠었는지 네가 아느냐
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 그 주초는 무엇 위에 세웠으며 그 모퉁이 돌은 누가 놓았었느냐
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 그 때에 새벽 별들이 함께 노래하며 하나님의 아들들이 다 기쁘게 소리하였었느니라
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 바닷물이 태에서 나옴 같이 넘쳐 흐를 때에 문으로 그것을 막은 자가 누구냐
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 그 때에 내가 구름으로 그 의복을 만들고 흑암으로 그 강보를 만들고
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 계한을 정하여 문과 빗장을 베풀고
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 이르기를 네가 여기까지 오고 넘어가지 못하리니 네 교만한 물결이 여기 그칠지니라 하였었노라
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 네가 나던 날부터 아침을 명하였었느냐 새벽으로 그 처소를 알게 하여
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 그것으로 땅끝에 비취게 하고 악인을 그 가운데서 구축한 일이 있었느냐
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 땅이 변화하여 진흙에 인친 것 같고 만물이 옷 같이 나타나되
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 악인에게는 그 빛이 금한바 되고 그들의 높이 든 팔이 꺾이느니라
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 네가 바다 근원에 들어갔었느냐 깊은 물밑으로 걸어 다녔었느냐
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 사망의 문이 네게 나타났었느냐 사망의 그늘진 문을 네가 보았었느냐
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 땅의 넓이를 네가 측량하였었느냐 다 알거든 말할지니라
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 광명의 처소는 어느 길로 가며 흑암의 처소는 어디냐
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 네가 능히 그 지경으로 인도할 수 있느냐 그 집의 길을 아느냐
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 네가 아마 알리라 네가 그 때에 났었나니 너의 년수가 많음이니라
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 네가 눈 곳간에 들어갔었느냐 우박 창고를 보았느냐
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 내가 환난 때와 전쟁과 격투의 날을 위하여 이것을 저축하였노라
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 광명이 어느 길로 말미암아 뻗치며 동풍이 어느 길로 말미암아 땅에 흩어지느냐
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 누가 폭우를 위하여 길을 내었으며 우뢰의 번개 길을 내었으며
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 사람 없는 땅에, 사람 없는 광야에 비를 내리고
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 황무하고 공허한 토지를 축축하게 하고 연한 풀이 나게 하였느냐
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 비가 아비가 있느냐 이슬 방울은 누가 낳았느냐
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 얼음은 뉘 태에서 났느냐 공중의 서리는 누가 낳았느냐
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 물이 돌 같이 굳어지고 해면이 어느니라
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 네가 묘성을 매어 떨기 되게 하겠느냐 삼성의 띠를 풀겠느냐
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 네가 열두 궁성을 때를 따라 이끌어 내겠느냐 북두성과 그 속한 별들을 인도하겠느냐
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 네가 하늘의 법도를 아느냐 하늘로 그 권능을 땅에 베풀게 하겠느냐
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 네 소리를 구름에 올려 큰 물로 네게 덮이게 하겠느냐
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 네가 번개를 보내어 가게 하되 그것으로 네게 우리가 여기 있나 이다 하게 하겠느냐
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 가슴 속의 지혜는 누가 준 것이냐 마음 속의 총명은 누가 준 것이냐
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 누가 지혜로 구름을 계수하겠느냐 누가 하늘의 병을 쏟아
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 티끌로 진흙을 이루며 흙덩이로 서로 붙게 하겠느냐
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 네가 암사자를 위하여 식물을 사냥하겠느냐 젊은 사자의 식량을 채우겠느냐
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 그것들이 굴에 엎드리며 삼림에 누워서 기다리는 때에니라
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 까마귀 새끼가 하나님을 향하여 부르짖으며 먹을 것이 없어서 오락가락 할 때에 그것을 위하여 먹을 것을 예비하는 자가 누구냐
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< 욥기 38 >