< 욥기 33 >

1 그런즉 욥이여 내 말을 들으며 나의 모든 말에 귀를 기울이기를 원하노라
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 내가 입을 여니 내 혀가 입에서 동하는구나
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 내 말이 내 마음의 정직함을 나타내고 내 입술이 아는 바를 진실히 말하리라
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 하나님의 신이 나를 지으셨고 전능자의 기운이 나를 살리시느니라
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 네가 할 수 있거든 일어서서 내게 대답하고 내 앞에 진술하라
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 나와 네가 하나님 앞에서 일반이니 나도 흙으로 지으심을 입었은즉
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 내 위엄으로는 너를 두렵게 하지 못하고 내 권세로는 너를 누르지 못하느니라
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 네가 실로 나의 듣는데 말하였고 나는 네 말소리를 들었느니라 이르기를
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 나는 깨끗하여 죄가 없고 허물이 없으며 불의도 없거늘
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 하나님이 나를 칠 틈을 찾으시며 나를 대적으로 여기사
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 내 발을 착고에 채우시고 나의 모든 길을 감시하신다 하였느니라
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 내가 네게 대답하리라 이 말에 네가 의롭지 못하니 하나님은 사람보다 크심이니라
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 하나님은 모든 행하시는 것을 스스로 진술치 아니하시나니 네가 하나님과 변쟁함은 어찜이뇨
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 사람은 무관히 여겨도 하나님은 한번 말씀하시고 다시 말씀하시되
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 사람이 침상에서 졸며 깊이 잠들 때에나 꿈에나 밤의 이상 중에
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 사람의 귀를 여시고 인치듯 교훈하시나니
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 이는 사람으로 그 꾀를 버리게 하려 하심이며 사람에게 교만을 막으려 하심이라
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 그는 사람의 혼으로 구덩이에 빠지지 않게 하시며 그 생명으로 칼에 멸망치 않게 하시느니라
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 혹시는 사람이 병상의 고통과 뼈가 늘 쑤심의 징계를 받나니
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 그의 마음은 식물을 싫어하고 그의 혼은 별미를 싫어하며
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 그의 살은 파리하여 보이지 아니하고 보이지 않던 뼈가 드러나서
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 그의 혼이 구덩이에, 그의 생명이 멸하는 자에게 가까와지느니라
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 그럴 때에 만일 일천 천사 가운데 하나가 그 사람의 해석자로 함께 있어서 그 정당히 행할 것을 보일진대
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 하나님이 그 사람을 긍휼히 여기사 이르시기를 그를 건져서 구덩이에 내려가지 않게 하라 내가 대속물을 얻었다 하시리라
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 그런즉 그 살이 어린 아이보다 연하여져서 소년 때를 회복할 것이요
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 그는 하나님께 기도하므로 하나님이 은혜를 베푸사 그로 자기의 얼굴을 즐거이 보게 하시고 사람에게 그 의를 회복시키시느니라
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 그가 사람 앞에서 노래하여 이르기를 내가 전에 범죄하여 시비를 바꾸었으나 내게 무익하였었구나
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 하나님이 내 영혼을 건지사 구덩이에 내려가지 않게 하셨으니 내생명이 빛을 보겠구나 하리라
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 하나님이 사람에게 이 모든 일을 재삼 행하심은
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 그 영혼을 구덩이에서 끌어 돌이키고 생명의 빛으로 그에게 비취려 하심이니라
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 욥이여 귀를 기울여 내게 들으라 잠잠하라 내가 말하리라
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 만일 할 말이 있거든 대답하라 내가 너를 의롭게 하려 하노니 말하라
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 만일 없으면 내 말을 들으라 잠잠하라 내가 지혜로 너를 가르치리라
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< 욥기 33 >