< 예레미야 49 >

1 암몬 자손에 대한 말씀이라 여호와께서 이같이 말씀하시되 이스라엘이 무자하냐 상속자가 없느냐 말감이 갓을 점령하며 그 백성이 그 성읍들에 거함은 어찜이뇨
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 그러므로 나 여호와가 말하노라 보라, 날이 이르리니 내가 전쟁 소리에 암몬 자손의 랍바에 들리게 할 것이라 랍바는 거친 무더기가 되겠고 그 촌락들은 불에 탈 것이며 그 때에 이스라엘은 자기를 점령하였던 자를 점령하리라 여호와의 말이니라
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 헤스본아! 애곡할지어다 아이가 황폐하였도다 너희 랍바의 딸들아! 부르짖을지어다 굵은 베를 감고 애통하며 울타리 가운데서 앞 뒤로 달릴지어다 말감과 그 제사장들과 그 방백들이 다 사로 잡혀 가리로다
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 타락한 딸아! 어찌하여 골짜기 곧 네 흐르는 골짜기로 자랑하느냐 네가 어찌하여 재물을 의뢰하여 말하기를 누가 내게 오리요 하느냐
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 주 만군의 여호와가 말하노라 보라, 내가 두려움을 네 사방에서 네게 오게 하리니 너희 각 사람이 쫓겨서 바로 나갈 것이요 도망하는 자들을 모을 자가 없으리라
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 그러나 그 후에 내가 암몬 자손의 포로로 돌아오게 하리라 여호와의 말이니라 하시니라
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 에돔에 대한 말씀이라 만군의 여호와께서 이같이 말씀하시되 데만에 다시는 지혜가 없게 되었느냐 명철한 자에게 모략이 끊어졌느냐 그들의 지혜가 없어졌느냐
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 드단 거민아! 돌이켜 도망할지어다 깊은데 숨을지어다 내가 에서의 재난을 그에게 임하게 하여 그를 벌할 때가 이르게 하리로다
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 포도를 거두는 자들이 네게 이르면 약간의 열매도 남기지 아니하겠고 밤에 도적이 오면 그 욕심이 차기까지 멸하느니라
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 대저 내가 에서로 적신이 되게 하여 그 비밀한 곳들이 드러나게 하였나니 그가 그 몸을 숨길 수 없을 것이라 그 자손과 형제와 이웃이 멸망하였은즉 그가 없어졌느니라
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 네 고아들을 남겨 두라 내가 그들을 살려 두리라 네 과부들은 나를 의지할 것이니라
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 나 여호와가 이같이 말하노라 보라, 이 잔을 마시지 않을 자도 마시지 않지 못하겠거늘 네가 형벌을 온전히 면하겠느냐 면하지 못하고 반드시 마시리라
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 나 여호와가 말하노라 내가 나로 맹세하노니 보스라가 놀램과 저줏거리가 될 것이요 그 모든 성읍이 영영히 황폐하리라
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 내가 여호와에게서부터 오는 소식을 들었노라 사자를 열방 중에 보내어 이르시되 너희는 모여와서 그를 치며 일어나서 싸우라 하시도다
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 여호와께서 가라사대 내가 너를 열방 중에 작게 하였고 사람들 중에 멸시를 받게 하였느니라
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 바위 틈에 거하며 산꼭대기를 점령한 자여, 스스로 두려운 자인 줄로 여김과 네 마음의 교만이 너를 속였도다 네가 독수리같이 보금자리를 높이 지었을지라도 내가 거기서 너를 끌어 내리리라 여호와의 말이니라
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 에돔이 놀라운 것이 되리니 그리로 지나는 자마다 놀라며 그 모든 재앙을 인하여 비웃으리로다
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 나 여호와가 말하노라 소돔과 고모라와 그 이웃 성읍들의 멸망된 것같이 거기 거하는 사람이 없으며 그 중에 우거할 아무 인자가 없으리라
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 보라, 사자가 요단의 수풀에서 올라 오는 것같이 그가 와서 견고한 처소를 칠 것이라 내가 즉시 그들을 거기서 쫓아내고 택한 자를 내가 그 위에 세우리니 나와 같은 자 누구며 나로 더불어 다툴 자 누구며 내 앞에 설 목자가 누구뇨
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 그런즉 에돔에 대한 나 여호와의 도모와 데만 거민에 대하여 경영한 나 여호와의 뜻을 들으라 양떼의 어린 것들을 그들이 반드시 끌어가고 그 처소로 황무케 하리니
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 그 넘어지는 소리에 땅이 진동하며 그 부르짖는 소리는 홍해에 들리리라
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 보라, 원수가 독수리같이 날아와서 그 날개를 보스라 위에 펴는 그 날에 에돔 용사의 마음이 구로하는 여인 같으리라
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 다메섹에 대한 말씀이라 하맛과 아르밧이 수치를 당하리니 이는 흉한 소문을 듣고 낙담함이라 바닷가에 슬픔이 있고 평안이 없도다
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 다메섹이 피곤하여 몸을 돌이켜 달아나려 하니 떨림이 그를 움켰고 해산하는 여인같이 고통과 슬픔이 그를 잡았도다
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 찬송의 성읍, 나의 즐거운 성읍이 어찌 버린 것이 되지 않겠느냐?
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 나 만군의 여호와가 말하노라 그런즉 그 날에 그의 청년들은 그 거리에 엎드러지겠고 모든 군사는 멸절될 것이며
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 내가 다메섹의 성벽에 불을 놓으리니 벤하닷의 궁전이 살라지리라
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 바벨론 왕 느부갓네살에게 공격된 바 게달과 하솔 나라들에 대한 말씀이라 여호와께서 이같이 말씀하시되 너희는 일어나 게달로 올라가서 동방 자손들을 멸하라
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 너희는 그 장막과 양떼를 취하며 휘장과 모든 기구와 약대를 빼앗아다가 소유를 삼고 그들을 향하여 외치기를 두려움이 사방에 있다 할지니라
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 나 여호와가 말하노라 하솔 거민아! 도망하라 멀리 가서 깊은데 거하라 이는 바벨론 왕 느부갓네살이 너를 칠 모략과 너를 칠 계책을 정하였음이니라
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 나 여호와가 말하노라 너는 일어나 저 평안하고 염려없이 거하는 백성 곧 성문이나 문빗장이 없이 홀로 거하는 국민을 치라
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 그들의 약대들은 노략되겠고 그 많은 가축은 탈취를 당할 것이라 내가 그 머리털을 모지게 깍는 자들을 사면에 흩고 그 재난을 각 방에서 오게 하리라 여호와의 말이니라
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 하솔은 시랑의 거처가 되어 영원히 황무하리니 거기 거하는 사람이나 그 중에 우거하는 아무 인자가 없게 되리라
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 유다 왕 시드기야의 즉위한지 오래지 아니하여서 엘람에 대한 여호와의 말씀이 선지자 예레미야에게 임하니라 가라사대
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 나 만군의 여호와가 이같이 말하노라 보라, 내가 엘람의 힘의 으뜸되는 활을 꺽을 것이요
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 하늘의 사방에서부터 사방 바람을 엘람에 이르게 하여 그들을 사방으로 흩으리니 엘람에서 쫓겨난 자의 이르지 아니하는 나라가 없으리라
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 나 여호와가 말하노라 내가 엘람으로 그 원수의 앞, 그 생명을 찾는 자의 앞에서 놀라게 할 것이며 내가 재앙 곧 나의 진노를 그 위에 내릴 것이며 내가 또 그 뒤로 칼을 보내어 그를 진멸하기까지 할 것이라
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 내가 나의 위를 엘람에 베풀고 왕과 족장들을 그 곳에서 멸하리라 여호와의 말이니라
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 그러나 끝날에 이르러는 내가 엘람의 포로를 돌아오게 하리라 여호와의 말이니라
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< 예레미야 49 >