< 창세기 11 >

1 온 땅의 구음이 하나이요 언어가 하나이었더라
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 이에 그들이 동방으로 옮기다가 시날 평지를 만나 거기 거하고
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 서로 말하되 `자, 벽돌을 만들어 견고히 굽자' 하고 이에 벽돌로 돌을 대신하며 역청으로 진흙을 대신하고
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 또 말하되 `자, 성과 대를 쌓아 대 꼭대기를 하늘에 닿게 하여 우리 이름을 내고 온 지면에 흩어짐을 면하자' 하였더니
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 여호와께서 인생들의 쌓는 성과 대를 보시려고 강림하셨더라
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 여호와께서 가라사대 이 무리가 한 족속이요, 언어도 하나이므로 이같이 시작하였으니 이후로는 그 경영하는 일을 금지할 수 없으리로다
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 자, 우리가 내려가서 거기서 그들의 언어를 혼잡케 하여 그들로 서로 알아듣지 못하게 하자 하시고
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 여호와께서 거기서 그들을 온 지면에 흩으신 고로 그들이 성 쌓기를 그쳤더라
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 그러므로 그 이름을 바벨이라 하니 이는 여호와께서 거기서 온 땅의 언어를 혼잡케 하셨음이라 여호와께서 거기서 그들을 온 지면에 흩으셨더라
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 셈의 후예는 이러하니라 셈은 일백세 곧 홍수 후 이년에 아르박삿을 낳았고
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 아르박삿을 낳은 후에 오백년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 아르박삿은 삼십 오세에 셀라를 낳았고
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 셀라를 낳은 후에 사백 삼년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 셀라는 삼십세에 에벨을 낳았고
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 에벨을 낳은 후에 사백 삼년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 에벨은 삼십 사세에 벨렉을 낳았고
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 벨렉을 낳은 후에 사백 삼십년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 벨렉은 삼십세에 르우를 낳았고
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 르우를 낳은 후에 이백 구년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 르우는 삼십 이세에 스룩을 낳았고
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 스룩을 낳은 후에 이백 칠년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 스룩은 삼십세에 나홀을 낳았고
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 나홀을 낳은 후에 이백년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 나홀은 이십 구세에 데라를 낳았고
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 데라를 낳은 후에 일백 십 구년을 지내며 자녀를 낳았으며
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 데라는 칠십세에 아브람과, 나홀과, 하란을 낳았더라
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 데라의 후예는 이러하니라 데라는 아브람과, 나홀과, 하란을 낳았고 하란은 롯을 낳았으며
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 하란은 그 아비 데라보다 먼저 본토 갈대아 우르에서 죽었더라
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 아브람과 나홀이 장가 들었으니 아브람의 아내 이름은 사래며 나홀의 아내 이름은 밀가니 하란의 딸이요 하란은 밀가의 아비며 또 이스가의 아비더라
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 사래는 잉태하지 못하므로 자식이 없었더라
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 데라가 그 아들 아브람과 하란의 아들 그 손자 롯과 그 자부 아브람의 아내 사래를 데리고 갈대아 우르에서 떠나 가나안 땅으로 가고자 하더니 하란에 이르러 거기 거하였으며
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 데라는 이백 오세를 향수하고 하란에서 죽었더라
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

< 창세기 11 >