< Yakobo 5 >
1 Mwiinchage leno, mwevakavi, lilaga khusauti iya khwanya olwakhuva isida inchikhwiincha khulwume.
Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni.
2 Uvukavi wenyo vumangikhe ne mienda gwenyo gelesilwena mang'onyo amavivi.
Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu.
3 Ulutarama lwenyo ni ndala ma inchenyo inchilebila nu vunangi wainchene vulavoneha khulumwe nukhunanga emivele nu mwoto. Muvekhile ekhebana khenyo musikhu incha mwisho.
Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza.
4 Lolesyena, amahombo agavafomba mbombo-ava samuvahombile mbubeni wenyo- vilela! Ne khelelo ekhyavala avavabenile khefikhe mumbulokhuto incha mbakha va khepuga.
Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse.
5 Mutamile inchavunogwe ikherunga nukhwekhovosa mwevene mweyigotile inumbula inchenyo khusikhu inchaa khugeda.
Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa.
6 Mung'egile mubudile unyayelweli uyusibencha.
Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.
7 Leno mugegelanile, lokolo, alava ikhwiincha nkurudeva, inave ondemi igulela ovubeni wa lutalama ukhukhuma nkerunga, vuigulela ukhwumilela kwa mwene, uvutengulelo nu vumalelo wafula vuyitima.
Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza.
8 Umwe muviinchage vumeleli, mukasye inumbula incenyo, ulwa khuva ukhweincha khwa nkuludeva khufikhe.
Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera.
9 Valokolo mung'ung'uta yumwe khwayumwe, mulolage mulekhe ukhukhegiwa. Lola, ung'egi ikhwema pandwango.
Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!
10 Ikhekhwani, lolaga etabu nu wumeleli mwa nyamalago uvovakha inchovile nditawa lwankurudeva.
Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira.
11 Lola, tukhuvelanga vala avavikhwumlela, “huba.” Mupulikhe ukwiyumili ncha ulwa Ayubu, na mulumanyile ilisage elwa mbaha kwa Ayubu, khunjila yelekhu umbaha ade inchiwe ikisa nulusayo.
Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.
12 Khulikho fyoni, valokololwango, msite ukhwedyega, ama khukwanya au enkilunga, ama ukhwedyega khyokhyoni. Tena incha “Wejo” iyenyo yedekhane “Wejo” ne “mwikho” iyenyona yedekhane “Mwikho” mulolage mulagwela pasi pa vukhegi.
Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.
13 Khule yuyoni igati indyumwe ipata etabu? Yinogiwa adove. Je, umunu yoyoni ikhovokha? na ikhwemba ulwedayo.
Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza.
14 Mwe, khule munu igati indyumwe itamu? na avalenge avandwakho nivapelela vadove nu mwene, vape amafuta nditawa lwa mbaha,
Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye.
15 Nu ludovo ulwarwedekho luyavila utamu, nu mbaha ikhotanga inave iva avombile imbivi, uNguluve ikho syekhela.
Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa.
16 Lwa khuva imbivi inchenyo yumwe hwa yumwe, nukhudovelanila vemwene nu nino, mpate ukhupona, olwesayo.
Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.
17 UEliya ale munu nda masage ndufwe, adovile nu lwumelelo uhuta efula yesite okhutima na sayikhatime nkerunga osekhe ugwa mikha gedatu ne mienchi sita.
Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka.
18 Nu Eliya adovile tena, ne kherunga khwadulile ifula pakwanya pakherunga ne kherunga khekhava nuvubeni.
Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake.
19 Valokololwango, inave yoyoni igati indyufwe iyaga ukhukhuina khuyelweli, inave umunu uyunge khumbuincha,
Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza,
20 ulumanye yeyoni uvevukho ndongoja uvale ni mbivi ihegando gendo lwa mwene nu mbombo mbivi ikhutanga nafsi ya mwene ukhukhuma khwa vufwe nukhudendela imbivi ine honi.
kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.