< Ebhikolwa bhya Jintumwa 1 >

1 Echitabho cha kara nachandikile, ninaika gona ganu Yesu ambile okukora no kwiigisha,
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 okukinga olunaku olwo omwene okulamilwa ingulu. Gunu gwakolekene amalile okososha echilagilo okusoka ku Mwoyo Mwelu okuja Kuntumwa jinu asolele.
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 Ejire amara okunyasibhwa kwaye, omwene abhonekene kubhene ali muanga ne bhibharikisho bhyanfu nibhyolesha kutyo. Ku naku makumi gana eyolesishe ku bhene, na alomele ingulu yo bhukama bhwa Nyamuanga.
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 Bhuli akabhugangana amwi nabho, nabhakomeresha bhatasokao Yerusalemu, nawe bhalinde iahadi ya Latabhugenyi, eyo, aikile, “Mwonguwe okusoka kwanye
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 okubha Yohana abhatijaga chimwi kwa manji, nawe omubhatijibhwa kwo Mwoyo Omweru munaku jitali nyafu.”
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Mbe bhejire bhekofyanya amwi mbamubhusha, “Lata, gunu nigwo omwanya ogwokubhasubhisha Israeli obhukama?”
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 Omwene nabhabhwira, “Itali kwemwe okumenya omwanya ogwo Lata eteleyewo kubhukama bhwaye omwene.”
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 Nawe omulamila amanaga, akatungu ako Omwoyo Omweru kaja ingulu yemwe, nemwe omubha bhabhambasi bhani wona mu Yerusalemu na Bhuyaudi yona na Samaria no bhutelo bhwe chalo.”
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 Omukama Yesu ejile amara okwaika ganu, mbaroraga inguru, Omwene nagegibhwa inguru, elire ndimufundikila mbasingwa omurora kwa meso gebhwe.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 Omwanya nibharora mwiguru nekeneke nagenda, mbe, abhanu bhabhili mbemeleguru agati yebhwe bhafwaye jingubho jinyeru.
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 Mbaika, “Emwe abhanu bha Galilaya, okubhaki mwimeleguyu anu nimulorera mwinguru?” Unu Yesu oyo agegwa inguru mwiguru kasubha kwa injila iliya iliya lwa kutyo mwamurora nagenda mwiguru.
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Nio nibhasubha Yerusalemu okusoka muchima cha mizeituni echo chili ayeyi na Yerusalemu, olugendo rwa insiku ya isabhato.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 Bhejire bhakinga mbagenda mwigorofa eyo yaga bhekaye. Nabho ni Petro, Yohana, Yakobo, Andrea, Filipo, Thomaso, Batholomayo, Mathayo, Yakobo Omwana wa Alfayo, Simoni Zelote na Yuda Omwana wa Yakobo.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 Bhona nibhagwatana amwi lwa munu umwi, kwo kwikomesha nibhagenderera mwisabhwa. Amwi nabho bhaliga bhaliwo abhagasi, Mariamu Nyiramwene Yesu, na bhamura bhaye.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 Mu nsiku ejo Petro nemereguru agati ya bhaili, kuti bhanu 120, naika,
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 Bhaili, yaliga kwiire ati amaandiko gakumire, ao kara Omwoyo Omweru aikile kwo munwa gwa Daudi inguru ya Yuda, oyo abheresishe abho bhamugwatire Yesu.
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 Kwo kubha omwene ali umwi weswe na aramie orubhara lwaye lwa ifaida ku bhukosi bhunu.
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 (Mbe oli omunu unu agurire libhara kwicho aramie kwa mabhibhi gaye nao aguye atangasishe omutwe, omubhili ngwatika no bhura bhwaye bhwona mbubha abhweru mbwitika.
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 Bhona abho bhekaye Yerusalemu bhonguwe linu, kutyo orubhara orwo mbarubhilikila kwa inyaika yebhwe “Akeldama” eryo ni nsambu ya manyinga.”)
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 Mu chitabho cha Zaburi yandikirwe, 'Siga orubhara lwaye lubhe erugu na itekirisibhwa norwo umwi okwikara aliya;' na, 'Ikirisha omunu undi agege orubhara lwaye rwo bhutangasha.'
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 Eyo ni ya insonga, kutyo, umwi wa bharume abho bharubhishene neswe akatungu ako Omukama Yesu asokere no kwingira amwi neswe,
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 okwambira ku bhubhatija bhwa Yohana okukingira ku lusiku orwo agegerwe inguru, kwiire abhe mubhambasj wo bhusuruko amwi neswe.
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 “Mbatura imbele bharume bhabhili, Yusufu oyo atogwaga Barnaba, oyo ona abhilikirwagwa Yusto na Mathia.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 Abhene mbasabhwa mbaika ati, “Awe, Omukama, umenyere emitima ja abhanu bhona, kutyo tura abhweru ni uya ku bhaili bhanu oyo usorere
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 okugega olubhara mu bhukosi no bhutumwa, ao Yuda obhunyamuke no kugenda kurubhara rwaye.”
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 Mbabhuma jikura kwo lubhara rwebhwe, na ikura nimugwira Mathia oyo abharirwe amwi na bhaliya jintumwa ekumi na umwi.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

< Ebhikolwa bhya Jintumwa 1 >