< Izikeli 48 >
1 Hagi mopama refko hu'za nagate nofite'ma hu'za zamisaza naga'mofo zamagi'a amana hu'ne, Noti kaziga refaregama me'nea mopa Dani naga'mo erigahie. Hagi mopa atumpazamimo'a Hetloni kantega vuno Lebo-hamati vuteno, Damaskasi mopamofo atuparega Hamati tavaonte noti kaziga Hazar-enani uhanatigahie. E'ina hanigeno Dani mopamo'a zage hanati kazigatira evuno, zage fre kaziga evugahie.
“Nawa mayina a mafuko a Israeli: Dani adzakhala ndi chigawo chimodzi kuyambira kumalire akumpoto kuchokera ku nyanja kudzera ku Hetiloni mpaka ku chipata cha Hamati, kukafika ku Hazari-Enani, mzinda umene uli kumpoto kwa malire a Damasiko oyangʼanana ndi Hamati, kuchokera mʼchigawo chimodzi kummawa mpaka kumadzulo.
2 Hagi Dani nagamofo mopamo'ma ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Asa naga'mofo mopa megahie.
“Aseri adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi dziko la Dani kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
3 Hagi Asa nagamofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno, zage fre kazigama evaniana Naftali naga'mofo mopa megahie.
“Nafutali adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi dziko la Aseri kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
4 Hagi Naftali nagamofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Manase nagamofo mopa megahie.
“Manase adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi dziko la Nafutali kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
5 Hagi Manase nagamofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana Efraemi naga'mofo mopa megahie.
“Efereimu adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi dziko la Manase kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
6 Hagi Efraemi naga'mofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Rubeni naga'mofo mopa megahie.
“Rubeni adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi Efereimu kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
7 Hagi Rubeni naga'mofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana Juda naga'mofo mopa megahie.
“Yuda adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi Rubeni kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
8 Hagi Juda naga'mofo mopa atuparera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, ruotge musezane huta mopa regorintesageno megahie. Hagi ana mopamofo zaza'amo'ene atupa'amo'enena mago'a mopama regorinazankna huno mago avamenteke 90 kilomita hugahiankino, ana mopa atupamo'a zage hanati kazigati vuno zage fre kaziga uhanatigahie. E'ina hanigeno ana mopamofo amu'nompi mono nona megahie.
“Kuchita malire ndi Yuda kuchokera kummawa mpaka kumadzulo padzakhala chigawo chimene mudzachipereke ngati mphatso yapadera. Mulifupi mwake mudzakhala makilomita khumi ndi awiri ndi theka, ndipo mulitali mwake, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo, mudzafanana ndi zigawo zina za mafuko. Malo a Nyumba ya Mulungu adzakhala pakati pake.
9 Hagi ana mopamofo amu'nompima Ra Anumzamofoma regorimisaza mopamofo zaza'amo'a 90 kilomita hinkeno, atupa'amo'a 36 kilomita hugahie.
“Chigawo chapadera chimene mudzachipereke kwa Yehova mulitali mwake mudzakhala makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita asanu.
10 Hagi ana mopafinti'ma pristi vahetmima regorizmisaza mopamofo zaza'amo'a noti kaziga 90 kilomita hina, upa'amo'a zage fre kaziga 36 kilomita hina zage hanati kaziga 36 kilomita hina, sauti kaziga zaza'amo'a 90 kilomita hugahie. E'ina hanigeno Ra Anumzamofo ra mono nomo'a amu'nompi megahie.
Ichi chidzakhala chigawo chopatulika cha ansembe ndipo chidzagawidwe motere: Mbali ya kumpoto kutalika kwake kudzakhala makilomita khumi ndi awiri ndi theka, mbali ya kumadzulo kudzakhala makilomita asanu, mbali ya kummawa makilomita asanu ndiponso makilomita khumi ndi awiri ndi theka mbali yakummwera. Pakati pake padzakhala malo a Nyumba ya Mulungu.
11 E'i ana mopafima manisazana Sadoki nagapinti'ma fore'ma hu'nenaza pristi vahetaminke manigahaze. Na'ankure Israeli vahe'mo'zane mago'a Livae naga'mo'za hazaza hu'za natre'za namefira huonami'za, nagrira navariri fatgo hu'naze.
Chimenechi chidzakhala chigawo cha ansembe opatulika, ana a Zadoki, amene ndi okhulupirika ponditumikira Ine, ndipo sanasochere ngati momwe anachitira Alevi pamene Aisraeli anasochera.
12 Hagi pristi vahetmima regori zami'naza mopamo'a ruotge hugahiankino, Livae vahe'mokizmi mopamo'ma ome atre atupareti pristi vahera mopa regori zamigahaze.
Chigawochi, mwa zigawo zonse za mʼdzikomo, chidzakhala kwa ansembewo ngati mphatso yawo yapadera. Chidzachita malire ndi dziko la Alevi.
13 Hagi Livae naga'ma regori zamisaza mopamofo za'za'ane atupa'amo'enena, pristi vahetamimofo mopanena magozahu hugahie. Hagi anantarega mopamofo za'za'amo'a 90 kilomita hinkeno, atupa'amo'a 36 kilomita hugahie.
“Moyandikana ndi chigawo cha ansembe, Alevi adzakhala ndi dera lawo lotalika makilomita khumi ndi awiri ndi theka, ndipo mulifupi mwake makilomita asanu. Kutalika kwake konse kudzakhala makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita asanu.
14 Hagi magore huta pristi vahe'motane Livae vahemota ama ruotge'ma hu'nea mopa zagorera otrege mago'a zantera nona huta vahera ozamitfa hugahaze. Na'ankure ama ana mopamo'a ruotge hu'neakino, Ra Anumzamofo mopa megahie.
Asagulitse kapena kusinthitsa mbali iliyonse ya chigawo chimenechi. Ichi ndi chigawo chabwino kwambiri ndipo chisapatsidwe kwa anthu ena, chifukwa ndi chopatulikira Yehova.
15 Hagi ana ruotge'ma hu'nea mopafina sauti kaziga mago mopa regorintegahazankino, zaza'amo'a 90 kilomita hanigeno, atupa kaziga'amo'a 18 kilomita hugahie. E'i ana mopamo'a ruotgera osugosianki, ruga'a Israeli vahe'mo'za ana mopafina amne nona negi'za hoza antegahaze. Hagi e'i ana mopamofo amunompi rankumara megahie.
“Chigawo chotsala mulifupi mwake makilomita awiri ndi theka ndipo mulitali mwake makilomita khumi ndi awiri ndi theka, chidzakhala malo a anthu wamba, chomangapo nyumba ndiponso chodyetsera ziweto zawo. Mzinda udzamangidwa pomwepo ndipo udzakhala pakati ndi pakati.
16 Hagi ana rankuma'mofona 4'a asopa me'nigeno, ana maka asopamo'a 16.2 kilomita huno magozahu hugahie.
Miyeso yake ndi iyi: kumpoto kutalika kwake kudzakhala mamita 2,250, kummwera mamita 2,250, kummawa mamita 2,250 ndipo kumadzulo mamita 2,250.
17 Hagi ana rankumamofona megi'a hozama antesaza mopama meno kagi'nia mopamofona rama hu'amo'a 900 mita hugahie.
Chigawo cha mzinda chodyetsera ziweto chidzakhala motere: kumpoto kutalika kwake kudzakhala mamita 125, kummwera kutalika kwake kudzakhala mamita 125, kummawa kutalika kwake kudzakhala mamita 125, ndipo kumadzulo kutalika kwake kudzakhala mamita 125.
18 Hagi rankumamofoma zage hanati kaziga mopafine, zage fre kaziga mopafinena Jerusalemi kumapima manisaza vahe'mo'za hoza antegahaze. Hagi ana mopararemofo zazaznimo'a 36 kilo mita hanigeno, atupazanimo'a 18 kilomita hutere hugahie.
Chigawo chotsala, choyandikana ndi chigawo chopatulika, kutalika kwake makilomita asanu mbali yakummawa ndiponso makilomita asanu mbali ya kumadzulo. Dera limeneli lidzakhale lolimamo anthu ogwira ntchito mu mzinda.
19 Hagi mago mago Israeli nagapinti'ma e'za rankumapima eri'zama emeneri'za manisaza vahe'mo'za ana mopafina hoza antegahaze.
Anthu ogwira ntchito mu mzinda amene adzalime mʼmundamo adzachokera ku mafuko onse a Israeli.
20 Hagi ana maka erinte ruotge'ma hu'nea mopamofo za'za'amo'ene atupa'amo'enena, magozahu huno 90 kilomita hugahiankino ana mopamofo agu'afi ran kumara megahie.
Chigawo chopatulika chonsechi chidzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka mbali zonse. Ndiye kuti, mudzapatule padera chigawo chopatulika pamodzi ndi kadziko ka mzindawo.
21 Hagi erinte ruotge'ma hu mopafima ran kumama mesia mopamofo zage hanati kazigane, zage fre kazigama amnema me'nia mopa kini ne'mofo mopa megahie. Hagi zage hanati kazigama Jodani tinte'ma vu'nea mopane, zage fre kazigama Medeterenia Hagerinte'ma vu'nea mopamokea, noti kazigati uramino sauti kazigama vu'neana 90 kilo mita hutere hu'na'e.
“Tsono chigawo chotsala pambali zonse ziwiri za chigawo chopatulika ndi za kadziko ka mzinda, chikhale cha mfumu. Chidzayenda motere: kuyambira mʼmalire a chigawo chopatulika kukalekezera mʼmalire akummawa. Mbali ina kuyambiranso mʼmalire a chigawo chopatulika kukalekezera malire a kumadzulo, kudutsa kufupi ndi zigawo za mafuko. Dera lonselo likhale la mfumu.
22 Hagi kini ne'mofo mopamo'a Livae vahe'mokizmi mopane rankumama manesia mopamo'a rure megahie. Hagi ana hanigeno kini nemofo mopamofo agema'amo'a noti kaziga Juda nagamofo mopare ome atre'nigeno, sauti kaziga Benzameni naga'mofo mopare ome atregahie.
Choncho chigawo cha Alevi ndi chigawo cha mzinda zidzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzayambira mbali ya kummawa mpaka ya kumadzulo kwa dziko la Benjamini.
23 Hagi ruga'a Israeli naga'mo'za amana hu'za nagate nofitera hu'za mopa refko hu'za erigahaze. Hagi kini ne'mofo mopama sauti kazigama ome atretetira, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Benzameni naga'mokizmi mopa megahie.
“Za mafuko ena otsala zidzayenda motere: Benjamini adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzayambira mbali ya kummawa mpaka ya kumadzulo.
24 Hagi Benzameni naga'mofo mopama ome atresiretira, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Simioni nagamofo mopa megahie.
“Simeoni adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi chigawo cha Benjamini kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
25 Hagi Simioni naga'mofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Isaka naga'mofo mopa megahie.
“Isakara adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi chigawo cha Simeoni kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
26 Hagi Isaka naga'mofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Zebuluni naga'mofo mopa megahie
“Zebuloni adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi chigawo cha Isakara kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
27 Hagi Zebuluni naga'mofo mopama ome atresirera, zage hanati kazigati evuno zage fre kazigama evaniana, Gati naga'mofo mopa megahie.
“Gadi adzakhala ndi chigawo chimodzi. Chidzachita malire ndi chigawo cha Zebuloni kuchokera kummawa mpaka kumadzulo.
28 Hagi Gati nagamofo mopa atumpamo'a sauti kaziga Tamari kumateti agafa huno Mariba tinte Kadesi kumate vuteno, Isipi tinkraho avaririno vuno Medeterenia hagerinte uhanatigahie.
“Malire a Gadi a mbali yakummwera ku Negevi adzayenda kuchokera ku Tamara mpaka ku dziwe la Meriba Kadesi komanso kuchokera ku Mtsinje wa Igupto mpaka ku Nyanja Yayikulu.
29 Ama ana mopa Israeli naga'mokizmi refko huta zamisage'za, eri santihare'za manigahaze huno Ra Anumzana Mikozama Kegava Hu'nea Anumzamo'a hie.
“Ili ndilo dziko limene mudzagawire mafuko a Israeli kuti likhale cholowa. Zimenezi zidzakhala zigawo zawo, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
30 Hagi ama'i rankumapinti'ma atiramiza esaza kuma kafantaminkino, noti kaziga kuma keginamofo zaza'amo'a 2 tausen 250 mita hugahie.
“Izi ndizo zidzakhale zipata zotulukira mzinda, ndipo zidzatchulidwa mayina a mafuko a Israeli. Kuyambira kumpoto kumene kudzakhala kotalika mamita 2,250,
31 Hagi ana kumamofona 12fu'a kafa megahiankino, mago mago kafantera 12'a Israeli naga'mofo zamagi metere hugahie. Hagi noti kaziga 3'a kafa megahiankino, ese kafantera Rubeni agi mesigeno, anante kafantera Juda agi mesigeno, namba 3 kafantera Livae agi megahie.
kudzakhale zipata zitatu izi: cha Rubeni, cha Yuda ndi cha Levi.
32 Hagi zage hanati kaziga kuma keginamofo zaza'amo'a 2tausen 250mita hanigeno, 3'a kuma kafa megahie. Ese kafantera Josefe agi mesigeno, anante kafantera Benzameni agi mesigeno, namba 3 kafantera Dani agi megahie.
“Mbali ya kummawa, imene kutalika kwake ndi mamita 2,250, kudzakhala zipata zitatu izi: chipata cha Yosefe, chipata cha Benjamini ndi chipata cha Dani.
33 Hagi sauti kaziga kuma keginamofo zaza'amo'a 2 tausen 250 mita hanigeno, 3'a kuma kafa megahie. Ese kafantera Simioni agi mesigeno, anante kafantera Isaka agi mesigeno, nampa 3 kafantera Zebuluni agi megahie.
“Mbali yakummwera, imene kutalika kwake ndi mamita 2,250, kudzakhala zipata zitatu izi: chipata cha Simeoni, chipata cha Isakara ndi chipata cha Zebuloni.
34 Hagi zage fre kaziga kuma keginamofo zaza'amo'a, 2 tausen 250 mita hanigeno, 3'a kuma kafa megahie. Ese kafantera Gati agi mesigeno, anante kafantera Asa agi mesigeno, namba 3 kafantera Naftali agi megahie.
“Mbali ya kumadzulo, imene kutalika kwake ndi mamita 2,250 kudzakhala zipata zitatu izi: chipata cha Gadi, chipata cha Aseri ndi chipata cha Nafutali.
35 Hagi ana rankuma keginama rugagi'nea zaza'amo'a ana makara 9 tausen mita hugahie. Ana hina e'i ananknareti'ma agafama huno'ma vaniana, ana rankumamofo agi'a, Ra Anumzamo'a Amafi Mani'ne hu'za agi'a ahegahaze.
“Choncho kutalika kwa mzinda kuzungulira kwake kudzakhala mamita 9,000. “Ndipo dzina la mzindawo kuyambira nthawi imeneyo mpaka mʼtsogolo lidzakhala: Yehova Ali Pano.”