< 詩篇 97 >

1 主は王となられた。地は楽しみ、海に沿った多くの国々は喜べ。
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 雲と暗やみとはそのまわりにあり、義と正とはそのみくらの基である。
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 火はそのみ前に行き、そのまわりのあだを焼きつくす。
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 主のいなずまは世界を照し、地は見ておののく。
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 もろもろの山は主のみ前に、全地の主のみ前に、ろうのように溶けた。
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 もろもろの天はその義をあらわし、よろずの民はその栄光を見た。
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 すべて刻んだ像を拝む者、むなしい偶像をもってみずから誇る者ははずかしめをうける。もろもろの神は主のみ前にひれ伏す。
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 主よ、あなたのさばきのゆえに、シオンは聞いて喜び、ユダの娘たちは楽しむ。
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 主よ、あなたは全地の上にいまして、いと高く、もろもろの神にまさって大いにあがめられます。
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 主は悪を憎む者を愛し、その聖徒のいのちを守り、これを悪しき者の手から助け出される。
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 光は正しい人のために現れ、喜びは心の正しい者のためにあらわれる。
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 正しき人よ、主によって喜べ、その聖なるみ名に感謝せよ。
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.

< 詩篇 97 >