< 箴言 知恵の泉 26 >

1 誉が愚かな者にふさわしくないのは、夏に雪が降り、刈入れの時に雨が降るようなものだ。
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 いわれのないのろいは、飛びまわるすずめや、飛びかけるつばめのようなもので、止まらない。
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 馬のためにはむちがあり、ろばのためにはくつわがあり、愚かな者の背のためにはつえがある。
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 愚かな者にその愚かさにしたがって答をするな、自分も彼と同じようにならないためだ。
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 愚かな者にその愚かさにしたがって答をせよ、彼が自分の目に自らを知恵ある者と見ないためだ。
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 愚かな者に託して事を言い送る者は、自分の足を切り去り、身に害をうける。
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 あしなえの足は用がない、愚かな者の口には箴言もそれにひとしい。
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 誉を愚かな者に与えるのは、石を石投げにつなぐようだ。
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 愚かな者の口に箴言があるのは、酔った者が、とげのあるつえを手で振り上げるようだ。
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 通りがかりの愚か者や、酔った者を雇う者は、すべての人を傷つける射手のようだ。
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 犬が帰って来てその吐いた物を食べるように、愚かな者はその愚かさをくり返す。
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 自分の目に自らを知恵ある者とする人を、あなたは見るか、彼よりもかえって愚かな人に望みがある。
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 なまけ者は、「道にししがいる、ちまたにししがいる」という。
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 戸がちょうつがいによって回るように、なまけ者はその寝床で寝返りをする。
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 なまけ者は手を皿に入れても、それを口に持ってゆくことをいとう。
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 なまけ者は自分の目に、良く答えることのできる七人の者よりも、自らを知恵ありとする。
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 自分に関係のない争いにたずさわる者は、通りすぎる犬の耳をとらえる者のようだ。
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 隣り人を欺いて、「わたしはただ戯れにした」という者は、燃え木または矢、または死を、投げつける気違いのようだ。
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 たきぎがなければ火は消え、人のよしあしを言う者がなければ争いはやむ。
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 おき火に炭をつぎ、火にたきぎをくべるように、争いを好む人は争いの火をおこす。
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 人のよしあしをいう者の言葉はおいしい食物のようで、腹の奥にしみこむ。
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 くちびるはなめらかであっても、心の悪いのは上ぐすりをかけた土の器のようだ。
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 憎む者はくちびるをもって自ら飾るけれども、心のうちには偽りをいだく。
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 彼が声をやわらげて語っても、信じてはならない。その心に七つの憎むべきものがあるからだ。
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 たとい偽りをもってその憎しみをかくしても、彼の悪は会衆の中に現れる。
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 穴を掘る者は自らその中に陥る、石をまろばしあげる者の上に、その石はまろびかえる。
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 偽りの舌は自分が傷つけた者を憎み、へつらう口は滅びをきたらせる。
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< 箴言 知恵の泉 26 >