< 箴言 知恵の泉 10 >

1 ソロモンの箴言。知恵ある子は父を喜ばせ、愚かな子は母の悲しみとなる。
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 不義の宝は益なく、正義は人を救い出して、死を免れさせる。
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 主は正しい人を飢えさせず、悪しき者の欲望をくじかれる。
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 手を動かすことを怠る者は貧しくなり、勤め働く者の手は富を得る。
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 夏のうちに集める者は賢い子であり、刈入れの時に眠る者は恥をきたらせる子である。
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 正しい者のこうべには祝福があり、悪しき者の口は暴虐を隠す。
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 正しい者の名はほめられ、悪しき者の名は朽ちる。
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 心のさとき者は戒めを受ける、むだ口をたたく愚かな者は滅ぼされる。
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 まっすぐに歩む者の歩みは安全である、しかし、その道を曲げる者は災にあう。
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 目で、めくばせする者は憂いをおこし、あからさまに、戒める者は平和をきたらせる。
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 正しい者の口は命の泉である、悪しき者の口は暴虐を隠す。
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 憎しみは、争いを起し、愛はすべてのとがをおおう。
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 さとき者のくちびるには知恵があり、知恵のない者の背にはむちがある。
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 知恵ある者は知識をたくわえる、愚かな者のむだ口は、今にも滅びをきたらせる。
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 富める者の宝は、その堅き城であり、貧しい者の乏しきは、その滅びである。
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 正しい者の受ける賃銀は命に導き、悪しき者の利得は罪に至る。
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 教訓を守る者は命の道にあり、懲しめを捨てる者は道をふみ迷う。
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 憎しみを隠す者には偽りのくちびるがあり、そしりを口に出す者は愚かな者である。
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 言葉が多ければ、とがを免れない、自分のくちびるを制する者は知恵がある。
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 正しい者の舌は精銀である、悪しき者の心は価値が少ない。
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 正しい者のくちびるは多くの人を養い、愚かな者は知恵がなくて死ぬ。
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 主の祝福は人を富ませる、主はこれになんの悲しみをも加えない。
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 愚かな者は、戯れ事のように悪を行う、さとき人には賢い行いが楽しみである。
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 悪しき者の恐れることは自分に来り、正しい者の願うことは与えられる。
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 あらしが通りすぎる時、悪しき者は、もはや、いなくなり、正しい者は永久に堅く立てられる。
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 なまけ者は、これをつかわす者にとっては、酢が歯をいため、煙が目を悩ますようなものだ。
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 主を恐れることは人の命の日を多くする、悪しき者の年は縮められる。
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 正しい者の望みは喜びに終り、悪しき者の望みは絶える。
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 主は、まっすぐに歩む者には城であり、悪を行う者には滅びである。
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 正しい者はいつまでも動かされることはない、悪しき者は、地に住むことができない。
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 正しい者の口は知恵をいだし、偽りの舌は抜かれる。
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 正しい者のくちびるは喜ばるべきことをわきまえ、悪しき者の口は偽りを語る。
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< 箴言 知恵の泉 10 >