< ヨブ 記 34 >
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 「あなたがた知恵ある人々よ、わたしの言葉を聞け、あなたがた知識ある人々よ、わたしに耳を傾けよ。
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 口が食物を味わうように、耳は言葉をわきまえるからだ。
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 われわれは正しい事を選び、われわれの間に良い事の何であるかを明らかにしよう。
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 ヨブは言った、『わたしは正しい、神はわたしの公義を奪われた。
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 わたしは正しいにもかかわらず、偽る者とされた。わたしにはとががないけれども、わたしの矢傷はいえない』と。
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 だれかヨブのような人があろう。彼はあざけりを水のように飲み、
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 彼は言った、『人は神と親しんでも、なんの益もない』と。
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 それであなたがた理解ある人々よ、わたしに聞け、神は断じて悪を行うことなく、全能者は断じて不義を行うことはない。
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 神は人のわざにしたがってその身に報い、おのおのの道にしたがって、その身に振りかからせられる。
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 まことに神は悪しき事を行われない。全能者はさばきをまげられない。
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 だれかこの地を彼にゆだねた者があるか。だれか全世界を彼に負わせた者があるか。
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 神がもしその霊をご自分に取りもどし、その息をご自分に取りあつめられるならば、
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 すべての肉は共に滅び、人はちりに帰るであろう。
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 もし、あなたに悟りがあるならば、これを聞け、わたしの言うところに耳を傾けよ。
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 公義を憎む者は世を治めることができようか。正しく力ある者を、あなたは非難するであろうか。
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 王たる者に向かって『よこしまな者』と言い、つかさたる者に向かって、『悪しき者』と言うことができるであろうか。
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 神は君たる者をもかたより見られることなく、富める者を貧しき者にまさって顧みられることはない。彼らは皆み手のわざだからである。
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 彼らはまたたく間に死に、民は夜の間に振われて、消えうせ、力ある者も人手によらずに除かれる。
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 神の目が人の道の上にあって、そのすべての歩みを見られるからだ。
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 悪を行う者には身を隠すべき暗やみもなく、暗黒もない。
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 人がさばきのために神の前に出るとき、神は人のために時を定めておかれない。
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 彼は力ある者をも調べることなく打ち滅ぼし、他の人々を立てて、これに替えられる。
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 このように、神は彼らのわざを知り、夜の間に彼らをくつがえされるので、彼らはやがて滅びる。
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 彼は人々の見る所で、彼らをその悪のために撃たれる。
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 これは彼らがそむいて彼に従わず、その道を全く顧みないからだ。
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 こうして彼らは貧しき者の叫びを彼のもとにいたらせ、悩める者の叫びを彼に聞かせる。
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 彼が黙っておられるとき、だれが非難することができようか。彼が顔を隠されるとき、だれが彼を見ることができようか。一国の上にも、一人の上にも同様だ。
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 これは神を信じない者が世を治めることがなく、民をわなにかける事のないようにするためである。
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 だれが神に向かって言ったか、『わたしは罪を犯さないのに、懲しめられた。
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 わたしの見ないものをわたしに教えられたい。もしわたしが悪い事をしたなら、重ねてこれをしない』と。
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 あなたが拒むゆえに、彼はあなたの好むように報いをされるであろうか。あなたみずから選ぶがよい、わたしはしない。あなたの知るところを言いなさい。
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 悟りある人々はわたしに言うだろう、わたしに聞くところの知恵ある人は言うだろう、
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 『ヨブの言うところは知識がなく、その言葉は悟りがない』と。
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 どうかヨブが終りまで試みられるように、彼は悪人のように答えるからである。
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 彼は自分の罪に、とがを加え、われわれの中にあって手をうち、神に逆らって、その言葉をしげくする」。
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”