< ヨブ 記 19 >

1 そこでヨブは答えて言った、
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 「あなたがたはいつまでわたしを悩まし、言葉をもってわたしを打ち砕くのか。
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 あなたがたはすでに十度もわたしをはずかしめ、わたしを悪くあしらってもなお恥じないのか。
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 たといわたしが、まことにあやまったとしても、そのあやまちは、わたし自身にとどまる。
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 もしあなたがたが、まことにわたしに向かって高ぶり、わたしの恥を論じるならば、
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 『神がわたしをしえたげ、その網でわたしを囲まれたのだ』と知るべきだ。
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 見よ、わたしが『暴虐』と叫んでも答えられず、助けを呼び求めても、さばきはない。
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 彼はわたしの道にかきをめぐらして、越えることのできないようにし、わたしの行く道に暗やみを置かれた。
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 彼はわたしの栄えをわたしからはぎ取り、わたしのこうべから冠を奪い、
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 四方からわたしを取りこわして、うせさせ、わたしの望みを木のように抜き去り、
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 わたしに向かって怒りを燃やし、わたしを敵のひとりのように思われた。
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 その軍勢がいっせいに来て、塁を築いて攻め寄せ、わたしの天幕のまわりに陣を張った。
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 彼はわたしの兄弟たちをわたしから遠く離れさせられた。わたしを知る人々は全くわたしに疎遠になった。
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 わたしの親類および親しい友はわたしを見捨て、
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 わたしの家に宿る者はわたしを忘れ、わたしのはしためらはわたしを他人のように思い、わたしは彼らの目に他国人となった。
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 わたしがしもべを呼んでも、彼は答えず、わたしは口をもって彼に請わなければならない。
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 わたしの息はわが妻にいとわれ、わたしは同じ腹の子たちにきらわれる。
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 わらべたちさえもわたしを侮り、わたしが起き上がれば、わたしをあざける。
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 親しい人々は皆わたしをいみきらい、わたしの愛した人々はわたしにそむいた。
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 わたしの骨は皮と肉につき、わたしはわずかに歯の皮をもってのがれた。
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 わが友よ、わたしをあわれめ、わたしをあわれめ、神のみ手がわたしを打ったからである。
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 あなたがたは、なにゆえ神のようにわたしを責め、わたしの肉をもって満足しないのか。
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 どうか、わたしの言葉が、書きとめられるように。どうか、わたしの言葉が、書物にしるされるように。
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 鉄の筆と鉛とをもって、ながく岩に刻みつけられるように。
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 わたしは知る、わたしをあがなう者は生きておられる、後の日に彼は必ず地の上に立たれる。
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 わたしの皮がこのように滅ぼされたのち、わたしは肉を離れて神を見るであろう。
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 しかもわたしの味方として見るであろう。わたしの見る者はこれ以外のものではない。わたしの心はこれを望んでこがれる。
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 あなたがたがもし『われわれはどうして彼を責めようか』と言い、また『事の根源は彼のうちに見いだされる』と言うならば、
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 つるぎを恐れよ、怒りはつるぎの罰をきたらすからだ。これによって、あなたがたは、さばきのあることを知るであろう」。
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< ヨブ 記 19 >