< 詩篇 91 >
1 至上者のもとなる隠れたるところにすまふその人は全能者の蔭にやどらん
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 われヱホバのことを宣て ヱホバはわが避所わが城わがよりたのむ神なりといはん
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 そは神なんぢを狩人のわなと毒をながす疫癘よりたすけいだしたまふべければなり
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
4 かれその翮をもてなんぢを庇ひたまはん なんぢその翼の下にかくれん その眞實は盾なり干なり
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
6 幽暗にはあゆむ疫癘あり日午にはそこなふ勵しき疾あり されどなんぢ畏るることあらじ
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
7 千人はなんぢの左にたふれ萬人はなんぢの右にたふる されどその災害はなんぢに近づくことなからん
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
8 なんぢの眼はただこの事をみるのみ なんぢ惡者のむくいを見ん
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
9 なんぢ曩にいへりヱホバはわが避所なりと なんぢ至上者をその住居となしたれば
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 災害なんぢにいたらず苦難なんぢの幕屋に近づかじ
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 そは至上者なんぢのためにその使者輩におほせて 汝があゆむもろもろの道になんぢを守らせ給へばなり
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 彼ら手にてなんぢの足の石にふれざらんために汝をささへん
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 なんぢは獅と蝮とをふみ壯獅と蛇とを足の下にふみにじらん
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
14 彼その愛をわれにそそげるがゆゑに我これを助けん かれわが名をしるがゆゑに我これを高處におかん
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 かれ我をよはば我こたへん 我その苦難のときに偕にをりて之をたすけ之をあがめん
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 われ長寿をもてかれを足はしめ且わが救をしめさん
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”