< 箴言 知恵の泉 5 >

1 我が子よわが智慧をきけ 汝の耳をわが聰明に傾け
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 しかしてなんぢ謹愼を守り汝の口唇に知識を保つべし
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 娼妓の口唇は蜜を滴らし 其口は脂よりも滑なり
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 されど其終は茵蔯の如くに苦く兩刃の劍の如くに利し
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 その足は死に下り その歩は陰府に趣く (Sheol h7585)
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
6 彼は生命の途に入らず 其徑はさだかならねども自ら之を知ざるなり
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 小子等よいま我にきけ 我が口の言を棄つる勿れ
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 汝の途を彼より遠く離れしめよ 其家の門に近づくことなかれ
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 恐くは汝の榮を他人にわたし 汝の年を憐憫なき者にわたすにいたらん
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 恐くは他人なんぢの資財によりて盈され 汝の勞苦は他人の家にあらん
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 終にいたりて汝の身なんぢの體亡ぶる時なんぢ泣悲みていはん
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 われ敎をいとひ 心に譴責をかろんじ
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 我が師の聲をきかず 我を敎ふる者に耳を傾けず
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 あつまりの中會衆のうちにてほとんど諸の惡に陷れりと
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 汝おのれの水溜より水を飮み おのれの泉より流るる水をのめ
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 汝の流をほかに溢れしめ 汝の河の水を衢に流れしむべけんや
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 これを自己に歸せしめ 他人をして汝と偕にこに與らしむること勿れ
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 汝の泉に福祉を受しめ 汝の少き時の妻を樂しめ
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 彼は愛しき麀のごとく美しき鹿の如し その乳房をもて常にたれりとし その愛をもて常によろこべ
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 我子よ何なればあそびめをたのしみ 淫婦の胸を懐くや
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 それ人の途はヱホバの目の前にあり 彼はすべて其行爲を量りたまふ
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 惡者はおのれの愆にとらへられ その罪の繩に繋る
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 彼は訓誨なきによりて死 その多くの愚なることに由りて亡ぶべし
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

< 箴言 知恵の泉 5 >