< 箴言 知恵の泉 27 >
1 なんぢ明日のことを誇るなかれ そは一日の生ずるところの如何なるを知ざればなり
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 汝おのれの口をもて自ら讃むることなく人をして己を讃めしめよ 自己の口唇をもてせず 他人をして己をほめしめよ
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 石は重く沙は軽からず 然ど愚なる者の怒はこの二よりも重し
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 忿怒は猛く憤恨は烈し されど嫉妬の前には誰か立ことをを得ん
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 愛する者の傷つくるは眞實よりし 敵の接吻するは偽詐よりするなり
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 飽るものは蜂の蜜をも踐つく されど饑たる者には苦き物さへもすべて甘し
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 その家を離れてさまよふ人は その巣を離れてさまよふ鳥のごとし
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 膏と香とは人の心をよろこばすなり 心よりして勸言を與ふる友の美しきもまた斯のごとし
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 なんぢの友と汝の父の友とを棄るなかれ なんぢ患難にあふ日に兄弟の家にいることなかれ 親しき隣は疏き兄弟に愈れり
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 わが子よ智慧を得てわが心を悦ばせよ 然ば我をそしる者に我こたふることを得ん
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 賢者は禍害を見てみづから避け 拙者はすすみて罰をうく
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 人の保證をなす者よりは先その衣をとれ 他人の保證をなす者をば固くとらへよ
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 晨はやく起て大聲にその鄰を祝すれば却て呪詛と見なされん
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 これを制ふるものは風をおさふるがごとく 右の手に膏をつかむがごとし
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 無花果の樹をまもる者はその果をくらふ 主を貴ぶものは譽を得
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 水に照せば面と面と相肖るがごとく 人の心は人の心に似たり
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 陰府と沈淪とは飽ことなく 人の目もまた飽ことなし (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 坩堝によりて銀をためし鑢によりて金をためし その讃らるる所によりて人をためす
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 なんぢ愚なる者を臼にいれ杵をもて麥と偕にこれを搗ともその愚は去らざるなり
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 なんぢの羊の情况をよく知り なんぢの群に心を留めよ
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 富は永く保つものにあらず いかで位は世々にたもたん
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 羔羊はなんぢの衣服を出し 牝羊は田圃を買ふ價となり
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 牝羊の乳はおほくして汝となんぢの家人の糧となり汝の女をやしなふにたる
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.