< 箴言 知恵の泉 25 >

1 此等もまたソロモンの箴言なり ユダの王ヒゼキヤに屬せる人々これを輯めたり
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 事を隱すは神の榮譽なり 事を窮むるは王の榮譽なり
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 天の高さと地の深さと 王たる者の心とは測るべからず
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 銀より渣滓を除け さらば銀工の用ふべき器いでん
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 王の前より惡者をのぞけ 然ばその位義によりて堅く立ん
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 王の前に自ら高ぶることなかれ 貴人の場に立つことなかれ
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 なんぢが目に見る王の前にて下にさげらるるよりは ここに上れといはるること愈れり
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 汝かろがろしく出でて爭ふことなかれ 恐くは終にいたりて汝の鄰に辱しめられん その時なんぢ如何になさんとするか
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 なんぢ鄰と爭ふことあらば只これと爭へ 人の密事を洩すなかれ
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 恐くは聞者なんぢを卑しめん 汝そしられて止ざらん
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 機にかなひて語る言は銀の彫刻物に金の林檎を嵌たるが如し
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 智慧をもて譴むる者の之をきく者の耳におけることは 金の耳環と精金の飾のごとし
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 忠信なる使者は之を遣す者におけること穡收の日に冷かなる雪あるがごとし 能その主の心を喜ばしむ
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 おくりものすと偽りて誇る人は雨なき雲風の如し
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 怒を緩くすれば君も言を容る 柔かなる舌は骨を折く
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 なんぢ蜜を得るか 惟これを足る程に食へ 恐くは食ひ過して之を吐出さん
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 なんぢの足を鄰の家にしげくするなかれ 恐くは彼なんぢを厭ひ惡まん
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 その鄰に敵して虚偽の證をたつる人は斧刃または利き箭のごとし
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 艱難に遇ふとき忠實ならぬ者を賴むは惡しき歯または跛たる足を恃むがごとし
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 心の傷める人の前に歌をうたふは寒き日に衣をぬぐが如く 曹達のうへに酢を注ぐが如し
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 なんぢの仇もし饑ゑなば之に糧をくらはせ もし渇かば之に水を飮ませよ
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 なんぢ斯するは火をこれが首に積むなり ヱホバなんぢに報いたまふべし
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 北風は雨をおこし かげごとをいふ舌は人の顔をいからす
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 爭ふ婦と偕に室に居らんより屋蓋の隅にをるは宜し
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 遠き國よりきたる好き消息は渇きたる人における冷かなる水のごとし
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 義者の惡者の前に服するは井の濁れるがごとく泉の汚れたるがごとし
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 蜜をおほく食ふは善らず 人おのれの榮譽をもとむるは榮譽にあらず
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 おのれの心を制へざる人は石垣なき壞れたる城のごとし
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< 箴言 知恵の泉 25 >