< 箴言 知恵の泉 23 >

1 なんぢ侯たる者とともに坐して食ふときは 愼みて汝の前にある者の誰なるかを思へ
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 汝もし食を嗜む者ならば汝の喉に刀をあてよ
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 その珍饈を貧り食ふこと勿れ これ迷惑の食物なればなり
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 富を得んと思煩らふこと勿れ 自己の明哲を恃むこと勿れ
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 なんぢ虚しきに歸すべき者に目をとむるか 富はかならず自ら翅を生じて鷲のごとく天に飛さらん
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 惡目をする者の糧をくらふことなく その珍饈をむさぼりねがふことなかれ
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 そはその心に思ふごとくその人となりも亦しかればなり 彼なんぢに食へ飮めといふこといへどもその心は汝に眞實ならず
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 汝つひにその食へる物を吐出すにいたり 且その出しし懇懃の言もむなしくならん
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 愚なる者の耳に語ること勿れ 彼なんぢが言の示す明哲を藐めん
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 古き地界を移すことなかれ 孤子の畑を侵すことなかれ
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 そはかれが贖者は強し 必ず汝に對らひて之が訴をのべん
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 汝の心を敎に用ゐ 汝の耳を知識の言に傾けよ
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 子を懲すことを爲ざるなかれ 鞭をもて彼を打とも死ることあらじ
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 もし鞭をもて彼をうたばその霊魂を陰府より救ふことをえん (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 わが子よもし汝のこころ智からば我が心もまた歓び
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 もし汝の口唇ただしき事をいはば我が腎腸も喜ぶべし
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 なんぢ心に罪人をうらやむ勿れ ただ終日ヱホバを畏れよ
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 そは必ず應報ありて汝の望は廢らざればなり
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 わが子よ 汝ききて智慧をえ かつ汝の心を道にかたぶけよ
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 酒にふけり肉をたしむものと交ること勿れ
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 それ酒にふける者と肉を嗜む者とは貧しくなり 睡眠を貧る者は敞れたる衣をきるにいたらん
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 汝を生る父にきけ 汝の老たる母を軽んずる勿れ
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 眞理を買へ これを售るなかれ 智慧と誡命と知識とまた然あれ
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 義き者の父は大によろこび 智慧ある子を生る者はこれがために樂しまん
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 汝の父母を樂しませ 汝を生る者を喜ばせよ
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 わが子よ汝の心を我にあたへ 汝の目にわが途を樂しめ
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 それ妓婦は深き坑のごとく 淫婦は狭き井のごとし
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 彼は盗賊のごとく人を窺ひ かつ世の人の中に悖れる者を増なり
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 禍害ある者は誰ぞ 憂愁ある者は誰ぞ 爭端をなす者は誰ぞ 煩慮ある者は誰ぞ 故なくして傷をうくる者は誰ぞ 赤目ある者は誰ぞ
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 是すなはち酒に夜をふかすもの 往て混和せたる酒を味ふる者なり
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 酒はあかく盃の中に泡だち滑かにくだる 汝これを見るなかれ
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 是は終に蛇のごとく噬み蝮の如く刺すべし
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 また汝の目は怪しきものを見 なんぢの心は諕言をいはん
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 汝は海のなかに偃すもののごとく帆桅の上に偃すもののごとし
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 汝いはん人われを撃ども我いたまず 我を拷けども我おぼえず 我さめなばまた酒を求めんと
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< 箴言 知恵の泉 23 >