< 箴言 知恵の泉 17 >
1 睦じうして一塊の乾けるパンあるは あらそひありて宰れる畜の盈たる家に愈る
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 かしこき僕は恥をきたらする子ををさめ 且その子の兄弟の中にありて產業を分ち取る
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 銀を試むる者は坩堝 金を試むる者は鑢 人の心を試むる者はヱホバなり
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 惡を行ふものは虚偽のくちびるにきき 虚偽をいふ者はあしき舌に耳を傾ぶく
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 貧人を嘲るものはその造主をあなどるなり 人の災禍を喜ぶものは罪をまぬかれず
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 勝れたる事をいふは愚なる人に適はず 况て虚偽をいふ口唇は君たる者に適はんや
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 贈物はこれを受る者の目には貴き珠のごとし その向ふところにて凡て幸福を買ふ
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 愛を追求むる者は人の過失をおほふ 人の事を言ひふるる者は朋友をあひ離れしむ
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 一句の誡命の智人に徹るは百囘扑つことの愚なる人に徹るよりも深し
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 叛きもとる者はただ惡きことのみをもとむ 比故に彼にむかひて殘忍なる使者遣はさる
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 愚なる者の愚妄をなすにあはんよりは寧ろ子をとられたる牝熊にあへ
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 爭端の起源は堤より水をもらすに似たり この故にあらそひの起らざる先にこれを止むべし
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 惡者を義とし義者を惡しとするこの二の者はヱホバに憎まる
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 愚なる者はすでに心なし何ぞ智慧をかはんとて手にその價の金をもつや
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 朋友はいづれの時にも愛す 兄弟は危難の時のために生る
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 智慧なき人は手を拍てその友の前にて保證をなす
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 爭端をこのむ者は罪を好み その門を高くする者は敗壞を求む
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 邪曲なる心ある者はさいはひを得ず その舌をみだりにする者はわざはひに陷る
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 愚なる者を產むものは自己の憂を生じ 愚なる者の父は喜樂を得ず
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 心のたのしみは良薬なり 霊魂のうれひは骨を枯す
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 智慧は哲者の面のまへにあり されど愚なる者は目を地の極にそそぐ
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 愚なる子は其父の憂となり 亦これを生る母の煩勞となる
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 義者を罰するは善らず 貴き者をその義きがために扑は善らず
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 言を寡くする者は知識あり 心の靜なる者は哲人なり
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 愚なる者も默するときは智慧ある者と思はれ その口唇を閉るときは哲者とおもはるべし
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.