< ヨブ 記 7 >
1 それ人の世にあるは戰鬪にあるがごとくならずや 又其日は傭人の日のごとくなるにあらずや
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 奴僕の暮を冀がふが如く傭人のその價を望むがごとく
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 我は苦しき月を得させられ 憂はしき夜をあたへらる
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 我臥ば乃はち言ふ何時夜あけて我おきいでんかと 曙まで頻に輾轉ぶ
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 わが肉は蟲と土塊とを衣服となし 我皮は愈てまた腐る
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 わが日は機の梭よりも迅速なり 我望む所なくし之を送る
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 想ひ見よ わが生命が氣息なる而已 我目は再び福祉を見ること有じ
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 我を見し者の眼かさねて我を見ざらん 汝目を我にむくるも我は已に在ざるべし
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 雲の消て逝がごとく陰府に下れる者は重ねて上りきたらじ (Sheol )
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol )
10 彼は再びその家に歸らず 彼の郷里も最早かれを認めじ
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 然ば我はわが口を禁めず 我心の痛によりて語ひ わが神魂の苦しきによりて歎かん
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 我あに海ならんや鰐ならんや 汝なにとて我を守らせおきたまふぞ
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 わが牀われを慰め わが寢床わが愁を解んと思ひをる時に
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 汝夢をもて我を驚かし 異象をもて我を懼れしめたまふ
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 是をもて我心は氣息の閉んことを願ひ我この骨よりも死を冀がふ
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 われ生命を厭ふ 我は永く生るをことを願はず 我を捨おきたまへ 我日は氣のごときなり
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 人を如何なる者として汝これを大にし 之を心に留
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 朝ごとに之を看そなはし 時わかず之を試みたまふや
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 何時まで汝われに目を離さず 我が津を咽む間も我を捨おきたまはざるや
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 人を鑒みたまふ者よ我罪を犯したりとて汝に何をか爲ん 何ぞ我を汝の的となして我にこの身を厭はしめたまふや
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 汝なんぞ我の愆を赦さず我罪を除きたまはざるや 我いま土の中に睡らん 汝我を尋ねたまふとも我は在ざるべし
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”