< 創世記 9 >

1 神ノアと其子等を祝して之に曰たまひけるは生よ増殖よ地に滿よ
Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
2 地の諸の獸畜天空の諸の鳥地に匍ふ諸の物海の諸の魚汝等を畏れ汝等に懾かん是等は汝等の手に與へらる
Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
3 凡そ生る動物は汝等の食となるべし菜蔬のごとく我之を皆汝等に與ふ
Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
4 然ど肉を其生命なる其血のままに食ふべからず
“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
5 汝等の生命の血を流すをば我必ず討さん獸之をなすも人をこれを爲すも我討さん凡そ人の兄弟人の生命を取ば我討すべし
Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
6 凡そ人の血を流す者は人其血を流さん其は神の像のごとくに人を造りたまひたればなり
“Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
7 汝等生よ増殖よ地に饒くなりて其中に増殖よ
Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
8 神ノアおよび彼と偕にある其子等に告て言たまひけるは
Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
9 見よ我汝等と汝等の後の子孫
“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
10 および汝等と偕なる諸の生物即ち汝等とともなる鳥家畜および地の諸の獸と契約を立ん都て方舟より出たる者より地の諸の獸にまで至らん
pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
11 我汝等と契約を立ん總て肉なる者は再び洪水に絶るる事あらじ又地を滅す洪水再びあらざるべし
Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
12 神言たまひけるは我が我と汝等および汝等と偕なる諸の生物の間に世々限りなく爲す所の契約の徴は是なり
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
13 我わが虹を雲の中に起さん是我と世との間の契約の徴なるべし
Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
14 即ち我雲を地の上に起す時虹雲の中に現るべし
Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
15 我乃ち我と汝等および總て肉なる諸の生物の間のわが契約を記念はん水再び諸の肉なる者を滅す洪水とならじ
ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
16 虹雲の中にあらん我之を觀て神と地にある都て肉なる諸の生物との間なる永遠の契約を記念えん
Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
17 神ノアに言たまひけるは是は我が我と地にある諸の肉なる者との間に立たる契約の徴なり
Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
18 ノアの子等の方舟より出たる者はセム、ハム、ヤペテなりきハムはカナンの父なり
Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
19 是等はノアの三人の子なり全地の民は是等より出て蔓延れり
Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
20 爰にノアの農夫となりて葡萄園を植ることを始しが
Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
21 葡萄酒を飮て醉天幕の中にありて裸になれり
Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
22 カナンの父ハム其父のかくし所を見て外にありし二人の兄弟に告たり
Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
23 セムとヤペテ乃ち衣を取て倶に其肩に負け後向に歩みゆきて其父の裸體を覆へり彼等面を背にして其父の裸體を見ざりき
Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
24 ノア酒さめて其若き子の己に爲たる事を知れり
Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
25 是に於て彼言けるはカナン詛はれよ彼は僕輩の僕となりて其兄弟に事へん
anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
26 又いひけるはセムの神ヱホバは讚べきかなカナン彼の僕となるべし
Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
27 神ヤペテを大ならしめたまはん彼はセムの天幕に居住はんカナン其僕となるべし
Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
28 ノア洪水の後三百五十年生存へたり
Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
29 ノアの齡は都て九百五十年なりき而して死り
Anamwalira ali ndi zaka 950.

< 創世記 9 >