< 歴代誌Ⅰ 2 >
1 イスラエルの子等は左のごとしルベン、シメオン、レビ、ユダ、イツサカル、ゼブルン
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 ダン、ヨセフ、ベニヤミン、ナフタリ、ガド、アセル
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 ユダの子等はエル、オナン、シラなり この三人はカナンの女バテシユアがユダによりて生たるなり ユダの長子エルはヱホバの前に惡き事をなしたれば之を殺したまへり
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 ユダの媳タマルはユダによりてペレヅとゼラとを生りユダの子等は都合五人なりき
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 ゼラの子等はジムリ、エタン、ヘマン、カルコル、ダラ都合五人
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 カルミの子はアカル、アカルは詛はれし物につきて罪を犯してイスラエルを惱ませし者なり
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 ヘヅロンに生れたる子等はヱラメル、ラム、ケルバイ
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 ラム、アミナダブを生みアミナダブ、ナシヨンを生りナシヨンはユダの子孫の牧伯なり
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 ボアズ、オベデを生み、オベデ、ヱツサイを生り
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 ヱツサイの生る者は長子はエリアブ その次はアミナダブ その三はシヤンマ
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 かれらの姉妹はゼルヤとアビガル、ゼルヤの產る子はアビシヤイ、ヨアブ、アサヘルあはせて三人
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 アビガルはアマサを產り アサの父はイシマエル人ヱテルといふ者なり
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 ヘヅロンの子カレブはその妻アズバによりまたヱリオテによりて子を擧けたりその產る子等は左のごとし ヱシル、シヨバブおよびアルドン
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 アズバ死たればカレブまたエフラタを娶れり エフラタ、カレブによりてホルを產り
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 その後ヘヅロンはギレアデの父マキルの女の所にいれりその之を娶れる時は六十歳なりき彼ヘヅロンによりてセグブを產り
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 セグブ、ヤイルを生りヤイルはギレアデの地に邑二十三を有り
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 然るにゲシユルおよびアラム彼等よりヤイルの邑々およびケナテとその郷里など都合六十の邑を取り是皆ギレアデの父マキルの子等なりき
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 ヘヅロン、カレブエフテタに死て後ヘヅロンの妻アビヤその子アシユルを生りアシユルはテコアの父なり
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 ヘヅロンの長子ヱラメルの子等は長子はラム 次はブナ、オレン、オゼム、アヒヤ
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 ヱラメルはまた他の妻をもてりその名をアタラといふ彼はオナムの母なり
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 ヱラメルの長子ラムの子等はマアツ、ヤミン、エケル
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 オナムの子等はシヤンマイ、ヤダ、シヤンマイの子等はナダブおよびアビシユル
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 アビシユルの妻の名はアビハイルといふ彼アバンおよびモリデを生り
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 ナダブの子等はセレデおよびアツパイム、セレデは子なくして死り
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 アツパイムの子はイシ、イシの子はセシヤン、セシヤンの子はアヘライ
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 シヤンマイの兄弟ヤダの子はヱテルおよびヨナタン、ヱテルは子なくして死り
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 ヨナタンの子等はペレテおよびザザ、ヱラメルの子孫は斯のごとし
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 セシヤンは男子なくして惟女子ありしのみなるがセシヤンにヤルハと名くるエジプトの僕ありければ
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 セシヤンその女をこの僕ヤルハに與へて妻となさしめたり彼ヤルハによりてアツタイを生り
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 ザバデ、エフラルを生み エフラル、オベデを生み
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 オベデ、ヱヒウを生み ヱヒウ、アザリヤを生み
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 アザリヤ、ヘレヅを生み ヘレヅ、ヱレアサを生み
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 ヱレアサ、シスマイを生み シスマイ、シヤルムを生み
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 シヤルム、ヱカミヤを生み ヱカミヤ、エリシヤマを生り
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 ヱラメルの兄弟カレブの子等はその長子をメシヤといふ是はジフの父なり ジフの子はマレシヤ、マレシヤはヘブロンの父なり
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 ヘブロンの子等はコラ、タツプア、レケム、シマ
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 シマはラハムを生り ラハムはヨルカムの父なり レケムはシヤンマイを生り
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 シヤンマイの子はマオン、マオンはベテスルの父なり
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 カレブの妾エパでハラン、モザおよびガゼズを產り ハランはガゼズを生り
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 ヱダイの子等はレゲム、ヨタム、ゲシヤン、ペレテ、エバ、シヤフ
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 カレブの妾マアカはシベルおよびテルハナを生み
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 またマデマンナの父シヤフおよびマクベナとギベアの父シワを生り カレブの女子はアクサといふ
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 カレブの子孫は左のごとしエフラタの長子ホルの子はキリアテヤリムの父シヨバル
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 ベテレヘムの父サルマおよびベテカデルの父ハレフ
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 キリアタヤリムの父シヨバルの子等はハロエにメヌコテ人の半
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 またキリアテヤリムの宗族はイテリ族プヒ族シユマ族ミシラ族 是等よりザレア族およびエシタオル族出たり
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 サルマの子孫はベテレヘム、ネトバ族アタロテベテヨアブ、マナハテ族の半およびゾリ族
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 ならびにヤベヅに住る諸士の宗族すなはちテラテ族シメアテ族スカテ族是等はケニ人にしてレカブの家の先祖ハマテより出たる者なり
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.