< Salmi 88 >

1 Canto. Salmo dei figliuoli di Kore. Per il Capo de’ musici. Da cantarsi mestamente. Cantico di Heman, l’Ezrahita. O Eterno, Dio della mia salvezza, io grido giorno e notte nel tuo cospetto.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Venga la mia preghiera dinanzi a te, inclina il tuo orecchio al mio grido;
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 poiché l’anima mia è sazia di mali, e la mia vita è giunta presso al soggiorno dei morti. (Sheol h7585)
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol h7585)
4 Io son contato fra quelli che scendon nella fossa; son come un uomo che non ha più forza.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Prostrato sto fra i morti, come gli uccisi che giaccion nella tomba, de’ quali tu non ti ricordi più, e che son fuor della portata della tua mano.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Tu m’hai posto nella fossa più profonda, in luoghi tenebrosi, negli abissi.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 L’ira tua pesa su me, e tu m’hai abbattuto con tutti i tuoi flutti. (Sela)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Tu hai allontanato da me i miei conoscenti, m’hai reso un’abominazione per loro. Io son rinchiuso e non posso uscire.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 L’occhio mio si consuma per l’afflizione; io t’invoco ogni giorno, o Eterno, stendo verso te le mie mani.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Opererai tu qualche miracolo per i morti? I trapassati risorgeranno essi a celebrarti? (Sela)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 La tua benignità sarà ella narrata nel sepolcro, o la tua fedeltà nel luogo della distruzione?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Le tue maraviglie saranno esse note nelle tenebre, e la tua giustizia nella terra dell’oblìo?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Ma, quant’è a me, o Eterno, io grido a te, e la mattina la mia preghiera ti viene incontro.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Perché, o Eterno, rigetti tu l’anima mia? Perché nascondi il tuo volto da me?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Io sono afflitto, e morente fin da giovane; io porto il peso dei tuoi terrori e sono smarrito.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 I tuoi furori mi son passati addosso; i tuoi terrori m’annientano,
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 mi circondano come acque ogni giorno, mi attornian tutti assieme.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Hai allontanato da me amici e compagni; i miei conoscenti sono le tenebre.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

< Salmi 88 >