< Salmi 63 >

1 Salmo di Davide: quand’era nel deserto di Giuda. O Dio, tu sei l’Iddio mio, io ti cerco dall’alba; l’anima mia è assetata di te, la mia carne ti brama in una terra arida, che langue, senz’acqua.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Così t’ho io mirato nel santuario per veder la tua forza e la tua gloria.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Poiché la tua benignità val meglio della vita; le mie labbra ti loderanno.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Così ti benedirò finché io viva, e alzerò le mani invocando il tuo nome.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 L’anima mia sarà saziata come di midollo e di grasso, e la mia bocca ti loderà con labbra giubilanti.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 Quand’io mi ricordo di te sul mio letto, medito di te nelle veglie della notte.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Poiché tu sei stato il mio aiuto, ed io giubilo all’ombra delle tue ali.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 L’anima mia s’attacca a te per seguirti; la tua destra mi sostiene.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Ma costoro che cercano la rovina dell’anima mia, entreranno nelle parti più basse della terra.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Saran dati in balìa della spada, saranno la preda degli sciacalli.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Ma il re si rallegrerà in Dio; chiunque giura per lui si glorierà, perché la bocca di quelli che dicon menzogne sarà turata.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Salmi 63 >