< Salmi 49 >

1 Per il Capo de’ musici. De’ figliuoli di Core. Salmo. Udite questo, popoli tutti; porgete orecchio, voi tutti gli abitanti del mondo!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Imvani izi anthu a mitundu yonse; mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,
2 Plebei e nobili, ricchi e poveri tutti insieme.
anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika, olemera pamodzinso ndi osauka:
3 La mia bocca proferirà cose savie, e la meditazione del mio cuore sarà piena di senno.
Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru; mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.
4 Io presterò l’orecchio alle sentenze, spiegherò a suon di cetra il mio enigma.
Ndidzatchera khutu langa ku mwambo, ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.
5 Perché temerei ne’ giorni dell’avversità quando mi circonda l’iniquità dei miei insidiatori,
Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika, pamene achinyengo oyipa andizungulira.
6 i quali confidano ne’ loro grandi averi e si gloriano della grandezza delle loro ricchezze?
Iwo amene adalira kulemera kwawo ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?
7 Nessuno però può in alcun modo redimere il fratello, né dare a Dio il prezzo del riscatto d’esso.
Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.
8 Il riscatto dell’anima dell’uomo è troppo caro e farà mai sempre difetto.
Dipo la moyo ndi la mtengowapatali, palibe malipiro amene angakwanire,
9 Non può farsi ch’ei continui a vivere in perpetuo e non vegga la fossa.
kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya ndi kusapita ku manda.
10 Perché la vedrà. I savi muoiono; periscono del pari il pazzo e lo stolto e lasciano ad altri i loro beni.
Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira; opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.
11 L’intimo lor pensiero è che le loro case dureranno in eterno e le loro abitazioni d’età in età; dànno i loro nomi alle loro terre.
Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya, malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo, ngakhale anatchula malo mayina awo.
12 Ma l’uomo ch’è in onore non dura; egli è simile alle bestie che periscono.
Ngakhale munthu akhale wachuma chotani, adzafa ngati nyama.
13 Questa loro condotta è una follia; eppure i loro successori approvano i lor detti. (Sela)
Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha, ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula. (Sela)
14 Son cacciati come pecore nel soggiorno de’ morti; la morte è il loro pastore; ed al mattino gli uomini retti li calpestano. La lor gloria ha da consumarsi nel soggiorno de’ morti, né avrà altra dimora. (Sheol h7585)
Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda, ndipo imfa idzawadya. Olungama adzawalamulira mmawa; matupi awo adzavunda mʼmanda, kutali ndi nyumba zawo zaufumu. (Sheol h7585)
15 Ma Iddio riscatterà l’anima mia dal potere del soggiorno dei morti, perché mi prenderà con sé. (Sela) (Sheol h7585)
Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda; ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini. (Sheol h7585)
16 Non temere quand’uno s’arricchisce, quando si accresce la gloria della sua casa.
Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera, pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;
17 Perché, quando morrà, non porterà seco nulla; la sua gloria non scenderà dietro a lui.
Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira, ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.
18 Benché tu, mentre vivi, ti reputi felice, e la gente ti lodi per i godimenti che ti procuri,
Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala, ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,
19 tu te ne andrai alla generazione de’ tuoi padri, che non vedranno mai più la luce.
iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake, amene sadzaonanso kuwala.
20 L’uomo ch’è in onore e non ha intendimento è simile alle bestie che periscono.
Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru adzafa ngati nyama yakuthengo.

< Salmi 49 >