< Salmi 145 >

1 Salmo di lode. Di Davide. Io t’esalterò, o mio Dio, mio Re, benedirò il tuo nome in sempiterno.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Ogni giorno ti benedirò e loderò il tuo nome in sempiterno.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 L’Eterno è grande e degno di somma lode, e la sua grandezza non si può investigare.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Un’età dirà all’altra le lodi delle tue opere, e farà conoscer le tue gesta.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Io mediterò sul glorioso splendore della tua maestà e sulle tue opere maravigliose.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 E gli uomini diranno la potenza dei tuoi atti tremendi, e io racconterò la tua grandezza.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Essi proclameranno il ricordo della tua gran bontà, e canteranno con giubilo la tua giustizia.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 L’Eterno è misericordioso e pieno di compassione, lento all’ira e di gran benignità.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 L’Eterno è buono verso tutti, e le sue compassioni s’estendono a tutte le sue opere.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Tutte le tue opere ti celebreranno, o Eterno, e i tuoi fedeli ti benediranno.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Diranno la gloria del tuo regno, e narreranno la tua potenza
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 per far note ai figliuoli degli uomini le tue gesta e la gloria della maestà del tuo regno.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Il tuo regno è un regno eterno, e la tua signoria dura per ogni età.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 L’Eterno sostiene tutti quelli che cadono e rialza tutti quelli che son depressi.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Gli occhi di tutti sono intenti verso di te, e tu dài loro il loro cibo a suo tempo.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Tu apri la tua mano, e sazi il desiderio di tutto ciò che vive.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 L’Eterno è giusto in tutte le sue vie e benigno in tutte le sue opere.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 L’Eterno è presso a tutti quelli che lo invocano, a tutti quelli che lo invocano in verità.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Egli adempie il desiderio di quelli che lo temono, ode il loro grido, e li salva.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 L’Eterno guarda tutti quelli che l’amano, ma distruggerà tutti gli empi.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 La mia bocca proclamerà la lode dell’Eterno, e ogni carne benedirà il nome della sua santità, in sempiterno.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Salmi 145 >