< Salmi 128 >

1 Canto dei pellegrinaggi. Beato chiunque teme l’Eterno e cammina nelle sue vie!
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 Tu allora mangerai della fatica delle tue mani; sarai felice e prospererai.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 La tua moglie sarà come una vigna fruttifera nell’interno della tua casa; i tuoi figliuoli, come piante d’ulivo intorno alla tua tavola.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Ecco, così sarà benedetto l’uomo che teme l’Eterno.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 L’Eterno ti benedica da Sion, e vedrai il bene di Gerusalemme tutti i giorni della tua vita,
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 e vedrai i figliuoli dei tuoi figliuoli. Pace sia sopra Israele.
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Salmi 128 >